Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 7/14 tsamba 3-7
  • “Khalani Ndi Khalidwe Labwino Pakati pa Anthu a M’dzikoli”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • “Khalani Ndi Khalidwe Labwino Pakati pa Anthu a M’dzikoli”
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Nkhani Yofanana
  • Zofunika Kukumbukira pa Msonkhano Wachigawo wa 2015
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Khalidwe Lathu Labwino Limalemekeza Mulungu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Misonkhano Yathu Yachigawo Imafotokoza Mfundo za Choonadi
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2012
  • Masiku Atatu Otsitsimulidwa Mwauzimu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
km 7/14 tsamba 3-7

“Khalani Ndi Khalidwe Labwino Pakati pa Anthu a M’dzikoli”

1. N’chifukwa chiyani n’zofunika kuti tidzasonyeze khalidwe labwino pa nthawi ya msonkhano ukubwerawu?

1 Chaka chilichonse tikamachita msonkhano wachigawo, anthu savutika kuzindikira zimenezi. Choncho ndi bwino kuti khalidwe lathu lizikhala logwirizana ndi Mulungu amene timamulambira. (Lev. 20:26) Khalidwe komanso kavalidwe kathu, zizisonyeza kuti ndife otsatira enieni a Khristu. Pa nthawi ya msonkhano wachigawo kapena wa mayiko ukubwerawu, kodi tingatani kuti ‘tidzasonyeze khalidwe labwino pakati pa anthu a m’dzikoli,’ zomwenso zidzalemekeze Atate wathu wakumwamba?—1 Pet. 2:12.

2. Kodi pa nthawi ya msonkhano wachigawo, tingadzasonyeze makhalidwe achikhristu m’njira ziti?

2 Mudzasonyeze Makhalidwe Oyenera Mkhristu: Tikamakondana komanso kuchitira zabwino “anthu akunja,” timasonyeza kuti ndife osiyana ndi dzikoli. (Akol. 3:10; 4:5; 2 Tim. 3:1-5) Tiyenera kukhala okoma mtima komanso oleza mtima tikamachita zinthu ndi akuluakulu a m’mahotelo kapena ogwira ntchito m’malesitilanti. Tiyenera kuchita zimenezi ngakhale pa nthawi imene pabuka vuto linalake. Khalidwe labwino limaphatikizaponso kusiya kandalama kothokoza anthu ogwira ntchito palesitilanti, ngati anthu a kudera lathu amachita zimenezi.

3. Kodi makolo akukumbutsidwa kudzachita chiyani, ndipo n’chifukwa chiyani ayenera kudzachita zimenezi?

3 Makolo ayenera kumadzayang’anira ana awo pamalo a msonkhano, kumalesitilanti komanso kumalo ena. (Miy. 29:15) Woyang’anira wa pahotelo inayake anauza banja lina kuti: “Anthu inu timakukondani kwabasi. Ndinu anthu a makhalidwe abwino, ndi ana anu omwe. Anthu onse ogwira ntchito pahotelo pano akukamba za inu, ndipo tikulakalaka mutamabwera kumapeto kwa mlungu uliwonse.”

4. Pa nthawi ya msonkhano wachigawo, kodi ndi zinthu ziti zokhudza kavalidwe zomwe tiyenera kuziganizira?

4 Muzidzavala Modzilemekeza: Tikakhala pamalo a msonkhano tiyenera kuvala moyenera ndi modzilemekeza, osati motengera masitayilo a m’dzikoli. (1 Tim. 2:9) Ngakhale pamene tili kuhotelo kapena pamene tikupuma pambuyo pa pulogalamu ya tsikulo, sitiyenera kuvala motailira kapena kuvala zovala zolemba mawu osakhala bwino. Kuvala moyenera kudzachititsa kuti tisadzachite manyazi kuvala mabaji a msonkhano komanso kulalikira mwamwayi. Kuvala bwino ndiponso khalidwe lathu labwino pamene tili kumsonkhano, zidzathandiza kuti anthu a mitima yabwino amvetsere uthenga wa m’Baibulo komanso kuti alemekeze Yehova.—Zef. 3:17.

Zofunika Kukumbukira pa Msonkhano Wachigawo wa 2014

◼ Nthawi ya Msonkhano: Masiku onse atatu msonkhano uzidzayamba ndi nyimbo zomvetsera pa nthawi ya 8:20 m’mawa. Tonse tiyenera kudzakhala pansi pa nthawi imeneyi kuti msonkhano uyambe bwinobwino. Lachisanu ndi Loweruka msonkhano udzatha 3:55 madzulo, ndipo Lamlungu udzatha nthawi ya 2:50 chakumadzulo.

◼ Misonkhano ya Mayiko: M’madera ena mudzachitika msonkhano wa mayiko. Ngati abale ndi alongo ena angapite ku msonkhano woti sanaitanidwe, zingadzachititse kuti anthu adzapanikizane m’malo oterewa. Ngati pazifukwa zina mukufuna kukapezeka pa msonkhano wina, osati wa kudera lanu, chonde musadzapite ku msonkhano wa mayiko.

◼ Koimika Magalimoto: Malo onse ochitira msonkhano adzakhala ndi malo okwanira oimikako magalimoto ndi njinga. Tikukulimbikitsani kudzamvera zimene akalinde amene aikidwa kusamalira utumiki umenewu angakuuzeni. Eniake a magalimoto adzaonetsetse kuti zitseko za magalimoto ndi zokhoma. Nawonso eniake a njinga adzaonetsetse kuti njinga zawo n’zokhoma, asanakakhale pansi.

◼ Kusungirana Malo: Si bwino kukankhanakankhana pamalo a msonkhano n’cholinga choti ifeyo tikapeze malo abwino. Chikondi chimatichititsa kuti tiziganiziranso ena, ndipo izi zimasonyeza kuti ndife Akhristu oona komanso zimathandiza anthu ena kutamanda Mulungu. (Yoh. 13:34, 35; 1 Akor. 13:4, 5; 1 Pet. 2:12) Tingasungire malo anthu okhawo amene tabwera nawo pa galimoto imodzi, amene timakhala nawo nyumba imodzi kapena amene tikuphunzira nawo Baibulo. Padzakonzedwa malo okhala anthu okalamba, odwala ndi olumala. Popeza malo amenewa adzakhala ochepa, munthu mmodzi kapena awiri ndi amene ayenera kukhala ndi anthuwa, ngati pakufunika woti aziwasamalira.

◼ Chakudya Chamasana: Tikukulimbikitsani kuti mudzabwere ndi chakudya chamasana, m’malo mochoka pamalo a msonkhano kukagula chakudya pa nthawi yopuma. Mungatenge zakudya monga tchipisi, mpunga, mbatata, chinangwa ndi zakumwa. Koma mowa si wololedwa pamalo a msonkhano.

◼ Zopereka: Tingasonyeze kuyamikira ntchito yomwe inagwiridwa pokonzekera msonkhanowu, popereka mwa kufuna kwathu ndalama zothandiza ntchito ya padziko lonse. Polemba cheke, sonyezani kuti ndalamazo zikupita ku, “Association of Jehovah’s Witnesses of Malawi.”

◼ Mankhwala: Ngati mumamwa mankhwala enaake, muyenera kuonetsetsa kuti mwatenga okwanira chifukwa mankhwala amenewo sadzapezeka pa msonkhano. Anthu amene amadzibaya mankhwala a matenda a shuga ayenera kusamala mmene angataire masilenji. Sayenera kutaya m’mabini a pamalo a msonkhano kapenanso kungotaya pamene akhala.

◼ Kupewa Ngozi: Chonde yesetsani kupewa zinthu zimene zingachititse ngozi. Chaka chilichonse kumachitika ngozi ndipo zambiri za ngozi zimenezi zimachitika chifukwa chovala nsapato zazitali. Choncho, ndi bwino kuvala nsapato zimene mungathe kuyenda nazo bwinobwino.

◼ Ovutika Kumva: Nkhani za msonkhanowu zizidzamasuliridwa m’chinenero chamanja m’malo otsatirawa: Blantyre, Kasungu, Lilongwe, Luchenza, Magawa, Mangochi, Mzuzu, Nkhata Bay, Songani ndi malo enanso. Pa tsiku loyamba la msonkhanowu padzakhala chilengezo chonena za zimenezi.

◼ Zikuku ndi Njinga za Ana: Simukuyenera kubweretsa zinthu zimenezi pamalo a msonkhano.

◼ Perefyumu: Poganizira anthu amene, chifukwa cha mavuto ena, amadana ndi fungo lamphamvu, ndi bwino kusagwiritsa ntchito perefyumu wamphamvu kwambiri.—1 Akor. 10:24.

◼ Mafomu a Kaonaneni ndi Wachidwi Uyu (S-43): Pofotokoza za munthu aliyense amene anaonetsa chidwi mutamulalikira mwamwayi pa nthawi ya msonkhano, muzigwiritsa ntchito mafomu a S-43. Mungapereke mafomu osainidwa bwinobwino ku Dipatimenti ya Mabuku kapena kwa mlembi wa mpingo wanu mukabwera ku msonkhanowo.

◼ M’malesitilanti: Mukapita kulesitilanti muyenera kusonyeza khalidwe labwino chifukwa zimenezi zimalemekeza Yehova. Tiyenera kuvala zovala zoyenera Mkhristu.

◼ Foni za M’manja: Muyenera kuzitchera kuti zisalire, n’kusokoneza ena.

◼ Kujambula Mawu: Musadzalumikize zipangizo zanu zojambulira mawu ku magetsi kapena kuzokuzira mawu za pamsonkhano ndipo mudzasamale kuti zisasokoneze ena.

◼ Kujambula Zithunzi: Ngati mukujambula zithunzi, musagwiritse ntchito fulashi msonkhano uli m’kati.

◼ Utumiki Wodzipereka: Ngati mukufuna kudzachita nawo utumikiwu, mudzaonane ndi abale a ku Dipatimenti ya Antchito Odzipereka. Nawonso ana omwe akwanitsa zaka 16 angathe kuchita nawo utumikiwu moyang’aniridwa ndi makolo awo kapena munthu wina wachikulire wovomerezedwa ndi makolowo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena