Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 10/15 tsamba 3
  • Kubwereza za M’Sukulu ya Utumiki wa Mulungu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kubwereza za M’Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
km 10/15 tsamba 3

Kubwereza za M’Sukulu ya Utumiki wa Mulungu

Mafunso otsatirawa tidzawakambirana pa Sukulu ya Utumiki wa Mulungu, ya mlungu woyambira October 26, 2015.

  1. Kodi lemba la 2 Mafumu 13:18, 19 likusonyeza bwanji kuti kutumikira Mulungu mwakhama komanso ndi mtima wonse n’kofunika? [Sept. 7, w10 4/15 tsa. 26 ndime 11]

  2. Kodi ndani anali mfumu ya Isiraeli pa nthawi yomwe Yona anali mneneri, nanga zomwe zili pa 2 Mafumu 14:23-25 zikusonyeza bwanji kuti anagwira ntchito yake pa nthawi yovuta? [Sept. 7, w09 1/1 tsa. 25 ndime 4]

  3. Kodi Ahazi anasonyeza bwanji kuti sanakhulupirire zimene Yehova ananena kudzera mwa mneneri Yesaya? Nanga ifeyo tiyenera kudzifunsa funso liti tikamafuna kusankha zochita? (2 Maf. 16:7) [Sept. 14, w13 11/15 tsa. 17 ndime 5]

  4. Kodi ndi njira iti imene Rabisake anagwiritsa ntchito, yomwe imafanana ndi imene adani a anthu a Mulungu amagwiritsa ntchito masiku ano? Nanga ndi khalidwe liti lomwe lingatithandize kukana kutsatira mfundo za anthuwa? (2 Maf. 18:22, 25) [Sept. 14, w10 7/15 tsa. 13 ndime 3-4]

  5. Kodi chitsanzo cha Yosiya cha kudzichepetsa chingatithandize bwanji kuti tizipindula kwambiri tikamawerenga komanso kuphunzira Baibulo? (2 Maf. 22:19, 20) [Sept. 21, w00 3/1 tsa. 30 ndime 2]

  6. Kodi akatswiri ofukula zinthu zakale anapeza zinthu ziti, zomwe zikusonyeza kuti mafumu awiri otchulidwa pa 2 Mafumu 25:27-30 analikodi? [Sept. 28, w12 6/1 tsa. 5 ndime 2-3]

  7. Kodi Yabezi anapempha zinthu zitatu ziti kwa Yehova, nanga ifeyo tikuphunzirapo chiyani? (1 Mbiri 4:9, 10) [Oct. 5, w10 10/1 tsa. 23]

  8. Kodi zotsatira za nkhondo yotchulidwa pa 1 Mbiri 5:18-22 zingatilimbikitse bwanji kuti tipitirizebe kumenya nkhondo yathu yauzimu molimba mtima? [Oct. 12, w05 10/1 tsa. 9 ndime 7]

  9. Kodi n’chiyani chinathandiza Davide kumvetsa mfundo ya m’lamulo la Yehova pa nkhani ya kupatulika kwa magazi? Nanga tikuphunzira chiyani pa chitsanzo cha Davidechi? (1 Mbiri 11:17-19) [Oct. 19, w12 11/15 tsa. 6 ndime 12-14]

  10. Kodi Davide analephera kuchita chiyani pamene ankafuna kubweretsa likasa la pangano ku Yerusalemu? Nanga ifeyo tikuphunzira chiyani pa nkhani imeneyi? (1 Mbiri 15:13) [Oct. 26, w03 5/1 tsa. 10-11 ndime 11-13]

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena