Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 September tsamba 8
  • Zinthu Zimene Tiyenera Kupewa Tikamachititsa Phunziro la Baibulo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zinthu Zimene Tiyenera Kupewa Tikamachititsa Phunziro la Baibulo
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Muzithandiza Wophunzira Baibulo Kuti Abatizidwe
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2021
  • Kuphunzitsa M’njira Yosavuta
    Muzikonda Anthu—Muziwaphunzitsa
  • Mmene Tingapangire ophunzira ndi Buku la Chidziŵitso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1996
  • Kuchititsa Maphunziro a Baibulo Opita Patsogolo Gawo 2:
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 September tsamba 8

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Zinthu Zimene Tiyenera Kupewa Tikamachititsa Phunziro la Baibulo

Losindikizidwa
M’bale akulankhula kwambiri pamene akuphunzira ndi munthu

Tisamalankhule Kwambiri: Tikamachititsa phunziro la Baibulo, sitiyenera kufotokoza zinthu zambirimbiri. Yesu ankagwiritsa ntchito mafunso pofuna kuthandiza anthu kuganiza, n’cholinga choti adziwe zoyenera kuchita. (Mat. 17:24-27) Mafunso amathandiza kuti phunziro likhale losangalatsa. Amathandizanso kuti mudziwe ngati wophunzira wanu wamvetsa mfundo inayake komanso ngati akukhulupirira zimene waphunzirazo. (be 253 ndime 3-4) Mukafunsa funso, muzidikira kaye mpaka munthuyo atayankha. Ngati wophunzira wanuyo wayankha molakwika, sibwino kumuuza yankho lolondola. Mungamuthandize kupeza yankho lolondola pomufunsa mafunso owonjezera. (be 238 ndime 1-2) Musamalankhule mofulumira kwambiri n’cholinga choti wophunzira wanu asavutike kumvetsa mfundo zofunika.—be 230 ndime 4.

Mfundo zosatsatirika zofotokoza chifukwa chake timakalamba

Tisamafotokoze Zinthu Zambiri Nthawi Imodzi: Tikamachititsa phunziro, tiyenera kupewa kufotokoza zonse zimene tikudziwa pa nkhaniyo. (Yoh. 16:12) M’malo mochulutsa gaga m’diwa, tingachite bwino kuthandiza wophunzira wathu kumvetsa mfundo yaikulu ya ndime imene tikukambirana. (be 226 ndime 4-5) Nthawi zina, mfundo zowonjezera, ngakhale zitakhala zosangalatsa, zimangophimba mfundo zofunika. (be 235 ndime 3) Ngati wophunzirayo wamvetsa mfundo yaikulu, tingachite bwino kupita pa ndime ina.

M’bale akukamba zinthu zambirimbiri zomwe zikusokoneza munthu amene akumuphunzitsa Baibulo

Tisamangophunzitsa Kuti Tithane Nazo: Cholinga chathu tikamaphunzira ndi anthu chimakhala kuwafika pamtima, osati kuphunzira ndime zambiri. (Luka 24:32) Choncho tikamaphunzira, tingachite bwino kumawerenga Malemba omwe akugwirizana kwambiri ndi nkhaniyo. (2 Akor. 10:4; Aheb. 4:12; be 144 ndime 1-3) Tingachitenso bwino kumagwiritsa ntchito zitsanzo komanso mafanizo osavuta. (be  245 ndime 2-4) Tikamakonzekera, tingachite bwino kuganizira mavuto amene wophunzira wathu akukumana nawo komanso zimene amakhulupirira. Kenako tingasankhe mfundo zomwe zingamuthandize kwambiri. Mukamaphunzira naye, mungamufunse mafunso ngati awa: “Kodi mukukhulupirira kuti zimenezi n’zoona?” “Kodi zimenezi zikutiphunzitsa chiyani za Yehova?” “Kodi mfundo imeneyi ingakuthandizeni bwanji pamoyo wanu?”—be 238 ndime 3-5; 259 ndime 1.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena