Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb26 January tsamba 4-5
  • January 12-18

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • January 12-18
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2026
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2026
mwb26 January tsamba 4-5

JANUARY 12-18

YESAYA 21-23

Nyimbo Na. 120 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Kodi Tikuphunzira Chiyani pa Zimene Zinachitikira Sebina?

(10 min.)

Muzikhalabe odzichepetsa mukapatsidwa udindo (Yes 22:​15-19; w18.03 25 ¶7-9-mwbr)

Mukachotsedwa pa udindo musamasiye kutumikira Yehova mwakhama (Yes 36:3; w18.03 25 ¶10-mwbr)

Makolo kapena akulu, muzipereka malangizo a m’Malemba potsanzira mmene Yehova anachitira zinthu ndi Sebina (w18.03 26 ¶11-mwbr)

Zithunzi: M’bale akupatsidwa malangizo achikondi ndipo akulola kuti malangizowo amuumbe. 1. Zikumuvuta kulandira malangizo kuchokera kwa akulu awiri. 2. Akuwerenga Baibulo komanso kuganizira mozama zimene akuwerengazo. 3. Ali mu utumiki ndi mmodzi wa akulu omwe anamupatsa malangizo aja ndipo akusangalala.

Malangizo achikondi ndi njira imodzi imene Mulungu amagwiritsa ntchito potiumba

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Yes 21:1—N’chifukwa chiyani Babulo akutchulidwa kuti “chipululu chimene chili ngati nyanja”? (w06 12/1 11 ¶2-mwbr)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Yes 23:​1-14 (th phunziro 5)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(1 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Popanda kutchula mfundo ya m’Baibulo, pezani njira yomwe ingathandize munthu amene mukukambirana naye kudziwa kuti ndinu wa Mboni za Yehova (lmd phunziro 2, mfundo 4)

5. Ulendo Woyamba

(3 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Kambiranani mfundo ya choonadi yopezeka mu zakumapeto A, m’kabuku kakuti Muzikonda Anthu. (lmd phunziro 1, mfundo 3)

6. Ulendo Wobwereza

(2 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Munthuyo wakuuzani kuti watanganidwa. (lmd phunziro 7, mfundo 4)

7. Nkhani

(5 min.) ijwyp nkhani Na. 71-mwbr—Mutu: Kodi Ndingasankhe Bwanji Munthu Wabwino Woti Ndizimutsanzira? (th phunziro 9)

Bambo wina akuthandiza mnzake kudziwa kolowera pomwe ali pa mlatho. Anthu omwe ali pansi pawo akungoyendayenda kusowa kolowera.

Kutengera munthu wachitsanzo chabwino kungatithandize kukwaniritsa zolinga zathu

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 124

8. Zofunika Pampingo

(15 min.)

9. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) lfb mutu 52-53

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 3 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena