Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb26 March tsamba 12-13
  • April 20-26

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • April 20-26
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2026
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2026
mwb26 March tsamba 12-13

APRIL 20-26

YESAYA 54-55

Nyimbo Na. 86 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Kodi Inuyo Mupereka Chiyani?

(10 min.)

Yehova analonjeza kuti azidzaphunzitsa ana ake (Yes 54:13; w09 9/15 21 ¶3)

Muzigula choonadi pogwiritsa ntchito nthawi yanu (Yes 55:​1, 2; w18.11 4 ¶6-7)

Kumvetsera mwatcheru kumafuna khama, koma n’kothandiza kuti tidzapeze moyo (Yes 55:3; be 14 ¶3-5)

M’bale waimika dzanja kuti apereke ndemanga pamisonkhano.

DZIFUNSENI KUTI, ‘Ndingatani kuti ndizichita khama ndikamaphunzira pandekha?’

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Yes 54:17—Kodi mbali yoyamba ya vesili ikutikumbutsa mfundo zofunika zitatu ziti? (w19.01 6 ¶14-15)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Yes 54:​1-10 (th phunziro 11)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(2 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Kambiranani mfundo imodzi ya choonadi mu Zakumapeto A, m’kabuku kakuti Muzikonda Anthu. (lmd phunziro 1, mfundo 4)

5. Ulendo Woyamba

(2 min.) KULALIKIRA M’MALO OPEZEKA ANTHU AMBIRI. Kambiranani mfundo imodzi ya choonadi mu Zakumapeto A, m’kabuku kakuti Muzikonda Anthu. (lmd phunziro 2, mfundo 3)

6. Ulendo Wobwereza

(2 min.) KULALIKIRA M’MALO OPEZEKA ANTHU AMBIRI. M’patseni munthu limodzi mwa makadi athu. (lmd phunziro 9, mfundo 3)

7. Nkhani

(5 min.) be 28 ¶3–31 ¶2—Mutu: Kaphunziridwe Koyenera. (th phunziro 14)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 97

8. Musamalole Chilichonse Kukulepheretsani Kuphunzira Panokha

(15 min.) Nkhani yokambirana.

Mayi akuwerenga Baibulo m’mawa kwambiri mwana wake akugonabe.

Pali zinthu zambiri zimene zingamatilepheretse kuphunzira Baibulo patokha nthawi zonse. Tiyerekeze kuti mukufuna kuthandiza Mkhristu mnzanu yemwe akulephera kumaphunzira payekha mokhazikika kapena kuwerenga Baibulo tsiku lililonse. Iye wakuuzani zinthu zotsatirazi zomwe zikumulepheretsa. Pa vuto lililonse lembani njira imodzi, mfundo ya M’malemba kapena lifalensi imene ingamuthandize.

  • “Sindimawerenga bwino”

  • “Kuphunzira sikumandisangalatsa”

  • “Ndimasowa poyambira kuwerenga Baibulo komanso kuti ndiziwerenga zochuluka bwanji pa tsiku”

  • “Pali zambiri zoti n’kuphunzira, ndiye ndiziphunzira zinthu ziti mlungu uliwonse?”

  • “Ndimakhala ndi zochita zambiri moti n’zovuta kupeza nthawi yophunzira”

  • “Zimandivuta kuika maganizo pa zimene ndikuphunzira ndipo nthawi zina sindikumbukira zimene ndawerenga”

Onerani VIDIYO yakuti Kuphunzira Mwakhama. Kenako funsani funso ili:

  • Ndi mfundo ziti zokhudza kuphunzira patokha zomwe mwaona muvidiyoyi zimene zakusangalatsani?

9. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) lfb mutu 78-79

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 70 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2026)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena