Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g 7/15 tsamba 16
  • Nsagwada za Ng’ona

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Nsagwada za Ng’ona
  • Galamukani!—2015
  • Nkhani Yofanana
  • Kuona Ng’ona Pafupi
    Galamukani!—1995
  • Zamkatimu
    Galamukani!—2015
  • Wonyenga Wamkulu Wochokera—M’Zigama
    Galamukani!—1991
  • Kulankhula Momveka Bwino
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
Onani Zambiri
Galamukani!—2015
g 7/15 tsamba 16
Ng’ona yanyamula kamwana kake m’kamwa

KODI ZINANGOCHITIKA ZOKHA?

Nsagwada za Ng’ona

PA DZIKO LAPANSI palibe nyama yoluma mwamphamvu ngati ng’ona. Mwachitsanzo, ng’ona ina ya ku Australia ikaluma, mphamvu zake tingaziyerekezere ndi mphamvu za kuluma kwa mkango ndiyeno n’kuziwirikiza katatu. Koma nsagwadazi zikakhudzidwa, ng’onayo imazindikira mwamsanga kuposa mmene ifeyo timamvera tikakhudzidwa chala. Popeza khungu la ng’ona limakhala ngati chikhungwa, kodi zimenezi zimatheka bwanji?

Nsagwada zake zimakhala ndi timinyewa tina ting’onoting’ono timene timaithandiza. Katswiri wina dzina lake Duncan Leitch anachita kafukufuku wa timinyewa timeneti. Anati, “Timinyewati timachokera penapake m’chibade cha mutu wake.” Timasanjidwa m’njira yoti tikhale totetezeka komanso kuti ng’onayo izizindikira mwamsanga zinthu zimene zili m’kamwa. Choncho sivutika kudziwa kuti ichi n’chakudya, izi n’zinyalala. Ng’ona imathanso kutenga ana ake m’kamwa mwake osawaluma. Choncho tingati nsagwada za ng’ona n’zodabwitsa kwambiri.

Kodi inuyo mukuganiza bwanji? Kodi zinangochitika zokha kuti ng’ona ikhale ndi nsagwada zotere, kapena pali winawake amene anailenga?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena