Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 43
  • Yoswa Akhala M’tsongoleri

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yoswa Akhala M’tsongoleri
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Yehova Anasankha Yoswa
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Zimene Yoswa Anakumbukira
    Nsanja ya Olonda—2002
  • Mose Amenya Thanthwe
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Azondi 12
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 43

NKHANI 43

Yoswa Akhala M’tsongoleri

MOSE akufuna kulowa m’Kanani ndi Aisrayeli. Chotero akufunsa kuti: ‘Ndiloleni ndioloke Mtsinje wa Yordano, Yehova, ndi kuona dziko lokoma’li. Koma Yehova akuti: ‘Zakwanira, usaonjeze’nso kunena za izi ndi ine!’ Kodi mukudziwa chifukwa chake Yehova anatero?

N’chifukwa cha zimene zinachitika pamene Mose anamenya thanthwe. Pajatu, iye ndi Aroni sanalemekeze Yehova. Sanauze anthu kuti anali Yehova amene anali kutulutsa madzi m’thanthwe’lo. Chifukwa cha ichi Yehova anati sakawalola kulowa m’Kanani.

Chotero patapita miyezi yowerengeka pambuyo pa imfa ya Aroni, Yehova akuuza Mose kuti: ‘Tenga Yoswa, numuimike pamaso pa Eliezara wansembe ndi anthu. Ndipo pamenepo pamaso pa onse, uuze ali yense kuti Yoswa ndiye m’tsogoleri watsopano.’ Mose akuchita monga momwe’di Yehova akunenera, monga momwe mukuonera m’chithunzi’chi.

Ndiyeno Yehova akuuza Yoswa kuti: ‘Khala wamphamvu, nulimbe mtima; pakuti udzalowa nao ana a Israyeli m’dziko la Kanani limene ndiwalonjeza, ndipo ndidzakhala nawe.’

Kenako Yehova akuuza Mose kukwera pa Phiri la Nebo m’dziko la Moabu. Ali pamenepo Mose akutha kuona patsidya pa Mtsinje wa Yordano ndi kuona dziko la Kanani lokongola’lo. Yehova akuti: ‘Iri ndiro dziko limene ndinalonjeza kuninkha ana a Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Ndakuonetsa iri, koma sindidzakulola kulowamo.’

Mose akufera pa Phiri la Nebo pamenepo. Iye anali ndi zaka 120. Iye anali wamphamvube, ndipo maso ake anali kuonabe bwino. Anthu ali achisoni kwambiri ndipo akulira chifukwa chakuti Mose wafa. Koma ali okondwa kukhala ndi Yoswa monga m’tsogoleri wao watsopano.

Numeri 27:12-23; Deuteronomo 3:23-29; 31:1-8, 14-23; 32:45-52; 34:1-12.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena