Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 31
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Deuteronomo

      • Mose anali atatsala pangʼono kumwalira (1-8)

      • Kuwerenga Chilamulo pamaso pa anthu (9-13)

      • Yoswa anamuika kuti akhale mtsogoleri (14, 15)

      • Ananeneratu kuti Aisiraeli adzapandukira Mulungu (16-30)

        • Nyimbo yoti aphunzitse Aisiraeli (19, 22, 30)

Deuteronomo 31:2

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “kutuluka ndi kulowa.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 7:7; De 34:7; Mac 7:23
  • +Nu 20:12; De 3:27

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    10/1/2006, tsa. 31

Deuteronomo 31:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 9:3
  • +Nu 27:18; De 3:28; Yos 1:2

Deuteronomo 31:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 21:23, 24
  • +Nu 21:33, 35
  • +Eks 23:23

Deuteronomo 31:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 33:52; De 7:2, 24; 20:16

Deuteronomo 31:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yos 1:6; Sl 27:14; 118:6
  • +Nu 14:9; De 7:18
  • +De 4:31; Yos 1:5; Ahe 13:5

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    8/15/1998, ptsa. 10-11

Deuteronomo 31:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yos 10:25
  • +De 1:38

Deuteronomo 31:8

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 33:14
  • +Yos 1:9

Deuteronomo 31:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 34:27

Deuteronomo 31:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 15:1
  • +Le 23:34

Deuteronomo 31:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 16:16
  • +Ne 8:7

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    3/15/2007, tsa. 20

Deuteronomo 31:12

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “mʼmageti anu.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 4:10; Ahe 10:25

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    4/15/2010, tsa. 3

    9/15/2004, tsa. 27

    3/15/2000, tsa. 17

Deuteronomo 31:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 6:6, 7; Aef 6:4
  • +De 30:16

Deuteronomo 31:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 27:13
  • +De 3:28

Deuteronomo 31:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 33:9; 40:38

Deuteronomo 31:16

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “kugona pamodzi ndi makolo ako.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Owe 2:17; Sl 106:37-39
  • +1Mf 11:33
  • +Owe 2:12, 20

Deuteronomo 31:17

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 29:20
  • +1Mb 28:9; 2Mb 15:2; 24:20
  • +De 32:20; Sl 104:29; Eze 39:23
  • +Ne 9:27
  • +Owe 6:13

Deuteronomo 31:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yes 59:2

Deuteronomo 31:19

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “Muiike mʼkamwa mwawo.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 31:30; 32:44
  • +De 4:9; 11:19
  • +De 31:21

Deuteronomo 31:20

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “nʼkunenepa.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 15:18
  • +Eks 3:8; Nu 13:26, 27
  • +Ne 9:25
  • +Eks 24:7; De 8:12-14; 29:1; Ne 9:26

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kukambitsirana, tsa. 117

Deuteronomo 31:21

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 28:59
  • +Eks 16:4

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kukambitsirana, tsa. 117

Deuteronomo 31:23

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 27:18; De 31:14
  • +Yos 1:6, 9
  • +De 1:38; 3:28

Deuteronomo 31:24

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 34:27

Deuteronomo 31:26

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 17:18; 2Mb 34:14
  • +1Mf 8:9

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    7/15/1990, tsa. 28

Deuteronomo 31:27

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “kuuma khosi.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 9:24; Ne 9:26
  • +Eks 32:9; Sl 78:8

Deuteronomo 31:28

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 30:19

Deuteronomo 31:29

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Owe 2:19
  • +De 28:15

Deuteronomo 31:30

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 32:44

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 31:2Eks 7:7; De 34:7; Mac 7:23
Deut. 31:2Nu 20:12; De 3:27
Deut. 31:3De 9:3
Deut. 31:3Nu 27:18; De 3:28; Yos 1:2
Deut. 31:4Nu 21:23, 24
Deut. 31:4Nu 21:33, 35
Deut. 31:4Eks 23:23
Deut. 31:5Nu 33:52; De 7:2, 24; 20:16
Deut. 31:6Yos 1:6; Sl 27:14; 118:6
Deut. 31:6Nu 14:9; De 7:18
Deut. 31:6De 4:31; Yos 1:5; Ahe 13:5
Deut. 31:7Yos 10:25
Deut. 31:7De 1:38
Deut. 31:8Eks 33:14
Deut. 31:8Yos 1:9
Deut. 31:9Eks 34:27
Deut. 31:10De 15:1
Deut. 31:10Le 23:34
Deut. 31:11De 16:16
Deut. 31:11Ne 8:7
Deut. 31:12De 4:10; Ahe 10:25
Deut. 31:13De 6:6, 7; Aef 6:4
Deut. 31:13De 30:16
Deut. 31:14Nu 27:13
Deut. 31:14De 3:28
Deut. 31:15Eks 33:9; 40:38
Deut. 31:16Owe 2:17; Sl 106:37-39
Deut. 31:161Mf 11:33
Deut. 31:16Owe 2:12, 20
Deut. 31:17De 29:20
Deut. 31:171Mb 28:9; 2Mb 15:2; 24:20
Deut. 31:17De 32:20; Sl 104:29; Eze 39:23
Deut. 31:17Ne 9:27
Deut. 31:17Owe 6:13
Deut. 31:18Yes 59:2
Deut. 31:19De 31:30; 32:44
Deut. 31:19De 4:9; 11:19
Deut. 31:19De 31:21
Deut. 31:20Ge 15:18
Deut. 31:20Eks 3:8; Nu 13:26, 27
Deut. 31:20Ne 9:25
Deut. 31:20Eks 24:7; De 8:12-14; 29:1; Ne 9:26
Deut. 31:21De 28:59
Deut. 31:21Eks 16:4
Deut. 31:23Nu 27:18; De 31:14
Deut. 31:23Yos 1:6, 9
Deut. 31:23De 1:38; 3:28
Deut. 31:24Eks 34:27
Deut. 31:26De 17:18; 2Mb 34:14
Deut. 31:261Mf 8:9
Deut. 31:27De 9:24; Ne 9:26
Deut. 31:27Eks 32:9; Sl 78:8
Deut. 31:28De 30:19
Deut. 31:29Owe 2:19
Deut. 31:29De 28:15
Deut. 31:30De 32:44
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 31:1-30

Deuteronomo

31 Kenako Mose anapita kukauza Aisiraeli onse mawu awa, 2 kuti: “Tsopano ndili ndi zaka 120.+ Sindingathenso kukutsogolerani* chifukwa Yehova wandiuza kuti, ‘Suwoloka Yorodano uyu.’+ 3 Yehova Mulungu wanu akuwoloka patsogolo panu kuti akutsogolereni. Iye adzawononga mitundu imeneyi pamaso panu ndipo inu mudzaithamangitsa.+ Yoswa ndi amene akutsogolereni nʼkukuwolotsani,+ mogwirizana ndi zimene Yehova wanena. 4 Yehova adzachitira mitundu imeneyi zimene anachitira Sihoni+ ndi Ogi,+ mafumu a Aamori, ndiponso zimene anachitira dziko lawo pamene anawawononga.+ 5 Yehova adzakugonjetserani mitundu imeneyi, ndipo mudzaichitire mogwirizana ndi malamulo onse amene ndakupatsani.+ 6 Limbani mtima ndipo muchite zinthu mwamphamvu.+ Musawaope kapena kuchita nawo mantha,+ chifukwa Yehova Mulungu wanu ndi amene akuyenda patsogolo panu. Iye sadzakutayani kapena kukusiyani ngakhale pangʼono.”+

7 Kenako Mose anaitana Yoswa nʼkumuuza pamaso pa Aisiraeli onse kuti: “Limba mtima ndipo uchite zinthu mwamphamvu,+ chifukwa iwe ndi amene udzalowetse anthu awa mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo awo kuti adzawapatsa. Ndipo iwe ndi amene udzawagawire dzikolo kuti likhale cholowa chawo.+ 8 Yehova ndi amene akuyenda patsogolo panu ndipo apitiriza kuyenda nanu.+ Sadzakutayani kapena kukusiyani ngakhale pangʼono. Choncho musaope kapena kuchita mantha.”+

9 Kenako Mose analemba Chilamulo+ chimenechi nʼkuchipereka kwa ansembe, omwe ndi Alevi, amene amanyamula likasa la pangano la Yehova, komanso kwa akulu onse a Isiraeli. 10 Ndiyeno Mose anawalamula kuti: “Kumapeto kwa zaka 7 zilizonse, pa nthawi imene inaikidwiratu mʼchaka choti anthu angongole amasuke,+ Pachikondwerero cha Misasa,+ 11 Aisiraeli onse akabwera pamaso pa Yehova+ Mulungu wanu pamalo amene iye adzasankhe, muzidzawerenga Chilamulo ichi pamaso pa Aisiraeli onse kuti achimve.+ 12 Sonkhanitsani anthu,+ amuna, akazi, ana ndi alendo amene akukhala mʼmizinda yanu,* kuti amvetsere komanso kuti aphunzire zokhudza Yehova Mulungu wanu, kuti azimuopa ndiponso kuti azitsatira mosamala mawu onse a mʼChilamulo ichi. 13 Akatero ana awo amene sakudziwa Chilamulo ichi adzamvetsera+ ndipo adzaphunzira kuopa Yehova Mulungu wanu, masiku onse amene mudzakhale mʼdziko limene mukuwoloka Yorodano kukalitenga kuti likhale lanu.”+

14 Kenako Yehova anauza Mose kuti: “Taona, nthawi yoti ufe yayandikira.+ Itana Yoswa, ndipo mukaime pachihema chokumanako kuti ndikamuike kukhala mtsogoleri.”+ Choncho Mose ndi Yoswa anapita nʼkukaima pachihema chokumanako. 15 Ndiyeno Yehova anaonekera kuchihemako mʼchipilala cha mtambo chimene chinaima pafupi ndi khomo la chihema.+

16 Tsopano Yehova anauza Mose kuti: “Iweyo watsala pangʼono kufa,* ndipo anthu awa adzakhala osakhulupirika kwa ine ndipo adzayamba kulambira milungu yachilendo imene ili mʼdziko limene akupita.+ Iwo adzandisiya+ nʼkuphwanya pangano limene ndinapangana nawo.+ 17 Pa nthawi imeneyo mkwiyo wanga udzawayakira+ ndipo ndidzawasiya+ nʼkuwabisira nkhope yanga+ mpaka atawonongedwa.+ Ndiyeno akadzakumana ndi masoka komanso mavuto ambiri adzanena kuti, ‘Masoka amenewatu akutigwera chifukwa chakuti Mulungu wathu sali pakati pathu.’+ 18 Koma ine ndidzapitiriza kuwabisira nkhope yanga pa tsiku limenelo chifukwa cha zoipa zonse zimene achita, potembenukira kwa milungu ina.+

19 Tsopano mulembe nyimbo iyi+ nʼkuphunzitsa Aisiraeli.+ Muwaphunzitse* nyimbo imeneyi kuti ikhale mboni yanga pamaso pa Aisiraeliwo.+ 20 Ndikadzawalowetsa mʼdziko limene ndinalumbira kwa makolo awo,+ dziko loyenda mkaka ndi uchi,+ ndipo akadzadya nʼkukhuta, zinthu nʼkuyamba kuwayendera bwino,*+ adzatembenukira kwa milungu ina nʼkuyamba kuitumikira. Iwo adzandichitira mwano komanso kuphwanya pangano langa.+ 21 Ndiyeno akadzakumana ndi masoka komanso mavuto ambiri,+ nyimboyi idzawakumbutsa zimene ndinawachenjeza, (chifukwa mbadwa zawo sizikuyenera kuiwala nyimboyi), chifukwa ndikudziwa kale mtima umene ayamba kukhala nawo+ ndisanawalowetse nʼkomwe mʼdziko limene ndinawalumbirira.”

22 Choncho Mose analemba nyimboyi pa tsiku limenelo nʼkuphunzitsa Aisiraeli.

23 Ndiyeno Mulungu anaika Yoswa+ mwana wa Nuni kuti akhale mtsogoleri, ndipo anamuuza kuti: “Limba mtima ndipo uchite zinthu mwamphamvu,+ chifukwa iwe ndi amene udzalowetse Aisiraeli mʼdziko limene ndawalumbirira,+ ndipo ine ndidzapitiriza kukhala ndi iwe.”

24 Mose atangomaliza kulemba mawu onse a Chilamulo ichi mʼbuku,+ 25 Mose analamula Alevi amene amanyamula likasa la pangano la Yehova kuti: 26 “Tengani buku ili la Chilamulo+ ndipo muliike pambali pa likasa+ la pangano la Yehova Mulungu wanu, ndipo lidzakhala mboni ya Mulungu yokutsutsani. 27 Ineyo ndikudziwa bwino khalidwe lanu lopanduka+ ndi kuuma mtima* kwanu.+ Ngati mwakhala mukupandukira Yehova pamene ndili moyo, ndiye kuli bwanji pambuyo pa imfa yanga! 28 Sonkhanitsani akulu onse a mafuko anu ndi atsogoleri anu, kuti amve mawu awa amene ndikufuna kulankhula nawo, ndipo nditenge kumwamba ndi dziko lapansi kuti zikhale mboni zanga pamaso pawo.+ 29 Chifukwa ndikudziwa bwino kuti pambuyo pa imfa yanga, mosakayikira mudzachita zinthu zoipa+ nʼkupatuka kusiya njira imene ndakulamulani. Ndiyeno pamapeto pake tsoka lidzakugwerani,+ chifukwa mudzachita zoipa pamaso pa Yehova ndipo mudzamukhumudwitsa ndi ntchito za manja anu.”

30 Choncho mpingo wonse wa Isiraeli ukumva, Mose anayamba kulankhula mawu a nyimbo iyi, kuchokera poyambirira mpaka kumapeto kuti:+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena