Msonkhano wa Pachaka—October 6, 1990
MSONKHANO WA PACHAKA wa ziŵalo za Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania udzachitidwa pa October 6, 1990, pa Holo ya Msonkhano ya Mboni za Yehova, 2932 Kennedy Boulevard, Jersey City, New Jersey. Msonkhano woyambirira wa ziŵalo zokha udzasonkhanidwa pa 9:30 a.m., kutsatiridwa ndi msonkhano wa pachaka wachisawawa pa 10:00 a.m.
Ziŵalo za Corporation ziyenera kudziŵitsa Ofesi ya Mlembi tsopano kaamba ka kusintha kulikonse kwa makeyala awo olandirira makalata mkati mwa chaka chapita kotero kuti makalata okhazikika a chidziŵitso ndi masinthidwe angawafikire iwo mwamsanga itapita August 15.
Makalata amasinthidwewo, omwe adzatumizidwa kwa ziŵalo limodzi ndi chidziŵitso cha msonkhano wa pachaka, ayenera kubwezedwa kotero kuti afikire Ofesi ya Mlembi wa Sosaite posachedwera ndi September 1. Chiŵalo chirichonse chiyenera kudzaza ndi kubweza kalata yake ya masinthidwe mwamsanga, akumanena kaya iye adzakhalapo pamsonkhanowo mwaumwini kapena ayi. Chidziŵitso choperekedwa pa masinthidwe aliwonse chiyenera kukhala chotsimikizirika pa nsongayi, popeza chidzadaliridwa m’kugamulapo yemwe adzapezekapo mwaumwini.
Chikuyembekezeredwa kuti gawo lonse, kuphatikizapo msonkhano wa nthaŵi zonse wa za bizinesi ndi malipoti, zidzamalizidwa pofika 1:00 p.m. kapena mwamsanga pambuyo pake. Sipadzakhala gawo lamasana. Chifukwa cha kuchepa kwa malo, chivomerezo chidzakhalapo mwa tikiti yokha. Palibe makonzedwe amene adzapangidwa kaamba ka kulunzanitsa msonkhano wa pachaka ndi malaini a telefoni ku malo ena.