Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 2/02 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
Onani Zambiri
Utumiki wathu wa Ufumu—2002
km 2/02 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Feb. 15

“Kodi munafunsapo momwe mungatsogolere bwino moyo wanu ndiponso momwe mungasankhire bwino zinthu zofunika kwambiri? [Muyembekezeni ayankhe.] Ena mwa malangizo amene angakuthandizeni kuchita zimenezo, monga Lamulo la Chikhalidwe, amapezeka m’Baibulo. [Ŵerengani Mateyu 7:12.] Kodi ndi mfundo zachikhalidwe za Mulungu zina ziti zimene zingatithandize mwachindunji? Mudzapeza yankho m’magazini iyi.”

Galamukani! Mar. 8

“Mwina mwaona kuti masiku ano malo antchito ambiri aopsa zedi. Magazini iyi ili ndi malingaliro othandiza a momwe tingatetezere malo antchito. Ikusonyezanso kuti maganizo abwino amene timakhala nawo pantchito amakhudza thanzi lathu. Chonde mukaiŵerenge.”

Nsanja ya Olonda Mar. 1

“Ambirife tikuda nkhaŵa kuti kaya m’tsogolo muli zotani chifukwa cha zimene zikuchitika masiku ano. M’pemphero lotchuka, Yesu Kristu ananena chifukwa chake tingayembekeze tsogolo labwino. [Ŵerengani Mateyu 6:9, 10.] Anthu akuchitanso zolakwa zimene anthu akale ankachita. Koma nthaŵi imeneyo, amene anali kutumikira Mulungu anali ndi tsogolo labwino. Magazini iyi ikusonyeza momwe ifenso tingakhalire ndi tsogolo labwino.”

Galamukani! Mar. 8

“Baibulo limagogomezera kufunika kwa maphunziro abwino. [Ŵerengani Miyambo 2:10, 11.] Ambirife timadziŵa kuti n’kofunika kuti ana azikhala ndi aphunzitsi odziŵa bwino ntchito yawo. Galamukani! iyi ikufotokoza kufunika kwa ntchito ya aphunzitsi, momwe tingasonyezere kuyamikira zimene amachita, ndiponso zimene makolo angachite pothandiza aphunzitsi pantchito yawo yovutayi.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena