Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 3/03 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
km 3/03 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Mar. 15

“Kodi mukuganiza kuti ziphunzitso za Yesu ndi zothandiza m’nthaŵi yathu ino? [Yembekezani ayankhe.] Ndikukhulupirira mukugwirizana ndi lamulo limene Yesu anapereka pa tsiku lomaliza la moyo wake. [Ŵerengani Yohane 15:12.] Yesu anaphunzitsanso mfundo zabwino tsiku limenelo. Nsanja ya Olonda iyi ikusonyeza mmene ifeyo tingapindulire ndi zimenezo.”

Galamukani! Mar. 8

“Kodi mukuganiza kuti Mulungu anakonzeratu zoti anthu pamodzi ndi ana omwe, azivutika ndi matenda a kusowa kwa zakudya m’thupi? [Yembekezani ayankhe.] Taonani lonjezo lolimbikitsa ili lopezeka m’Baibulo. [Ŵerengani Salmo 72:16.] Magazini ya Galamukani! iyi ikufotokoza zimene zimachititsa mavuto akusowa kwa chakudya, ndiponso lonjezo la Mulungu lofunika kwambiri loti adzathetsa vutoli posachedwapa.”

Nsanja ya Olonda Apr. 1

“Zimene mukuziona apa ndi Mgonero wa Ambuye. [Onetsani tsamba loyamba ndi lomaliza la magazini.] Kodi mukudziŵa kuti ndi mwambo wokhawu umene Akristu amalamulidwa kukumbukira? [Yembekezani ayankhe. Kenako ŵerengani Luka 22:19.] Magazini iyi ikufotokoza ubwino wa mwambo umenewu ndiponso mmene umakukhudzirani.”

Galamukani! Mar. 8

“Chifukwa cha kubwera kwa mavidiyo a nyimbo, achinyamata ambiri amaonerera zinthu zachiwawa ndi zachiwerewere. Kodi mukuganiza kuti ndi bwino kuti achinyamata azionerera mavidiyo otero? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zimene Baibulo likunena pano za mmene Mulungu amaonera chiwawa. [Ŵerengani Salmo 11:5.] M’magazini iyi ya Galamukani!, muli nkhani imene ikufotokoza za mavidiyo a nyimbo.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena