Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 3/07 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
km 3/07 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda Mar. 15

“Anthu amalankhula kawirikawiri za kubwera kwa Yesu Khristu. Kodi mukuganiza kuti tikufunika kusangalala kapena kuda nkhawa ndi kubwera kwa Yesu kumeneku? [Yembekezani ayankhe.] Taonani mmene nkhaniyi inam’khudzira Yohane, amene analemba nawo Baibulo. [Werengani Chivumbulutso 22:20.] Magazini iyi ikufotokoza zimene zidzachitike Khristu akadzabwera.”

Galamukani! Mar.

“Zikuoneka kuti atsogoleri ambiri padzikoli ndi onyada kwambiri. Kodi mukuganiza kuti mtima woterewu umathandiza kuti dziko likhale pamtendere ndiponso logwirizana? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zimene Baibulo limanena pankhani ya kunyada. [Werengani Miyambo 16:18.] Nkhani iyi ikufotokoza ubwino wa kudzichepetsa.” M’sonyezeni nkhani yomwe yayambira pa tsamba 20.

Nsanja ya Olonda Apr. 1

“Pafupifupi tsiku lililonse timakhala ndi mafunso okhudza umoyo wathu, mabanja athu, ndiponso ntchito yathu. Kodi mukuganiza kuti mayankho odalirika ndiponso othandiza tingawapeze kuti? [Yembekezani ayankhe.] Taonani zimene Baibulo limanena pa 2 Timoteyo 3:16. [Werengani.] Magazini iyi ikufotokoza mmene Baibulo lingatithandizire m’njira zosiyanasiyana.”

Galamukani! Apr.

“M’madera ambiri, anthu akuona kuti makhalidwe a anthu akumka naipiraipira. Kodi inu mwaonapo zimenezi? [Yembekezani ayankhe.] Zinthu zimene tikuona masiku ano zikukwaniritsa ulosi wa m’Baibulo. [Werengani 2 Timoteyo 3:2-4.] Magazini iyi ikusonyeza zimene kuipiraipira kwa makhalidwe a anthu kukutanthauza ndiponso kuti mapeto ake n’chiyani.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena