Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 3/05 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
km 3/05 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda Mar. 15

“Anthu padziko lonse amalemekeza ziphunzitso za Yesu. [Werengani mawu ogwidwa patsamba 3, ndime 1.] Koma kodi mukuganiza kuti ziphunzitso zimenezo, monga chitsanzo chimene chili mu lemba ili, n’zothandiza masiku ano? [Werengani Mateyu 5:21, 22a. Ndiyeno yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza zimene Yesu anaphunzitsa ndi mmene tingapindulire nazo.”

Galamukani! Apr. 8

“Anthu ambiri amakonda mapiri chifukwa ndi okongola, koma kodi mumadziwa kuti mapiri amachirikiza moyo padziko lapansi lino? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza chifukwa chake timafunika mapiri ndiponso zimene zikuchitikira mapiri amenewa masiku ano. Ikufotokozanso mmene Mlengi adzatetezere mapiri amenewa.” Werengani Salmo 95:4.

Nsanja ya Olonda Apr. 1

“Kodi munamvapo zoti sayansi ndi Baibulo zimatsutsana? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza mbiri ya mkangano wa pakati pa sayansi ndi chipembedzo. Koma ikuperekanso umboni wosonyeza kuti sayansi yoona imagwirizana ndi Baibulo.” Muonetseni masamba 6 mpaka 7. Kenako werengani Mlaliki 1:7.

Galamukani! Apr. 8

“Kodi mukuganiza kuti makolo angachite chiyani kuti athandize ana awo kupewa mavuto pa zaka zawo za unyamata? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno werengani Yesaya 48:17, 18.] Magazini iyi ikulongosola mmene kugwiritsira ntchito malangizo a m’Baibulo kungathandizire makolo kulimbikitsa kulankhulana kwabwino ndi ana awo ndiponso kuwaikira malire oyenera.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena