Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 4/03 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
km 4/03 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Apr. 15

“Zaka zaposachedwapa anthu ambiri aona kuti moyo wauzimu ukuloŵa pansi. Kodi inunso mwaona zimenezi? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Salmo 119:105.] Moyo wauzimu ungathandize anthu kupeŵa mavuto ambiri pamoyo wawo. Magazini iyi ikutchula kumene tingapeze zinthu zimene zingatithandize kukhala ndi moyo wauzimu.”

Galamukani! Apr. 8

“Kodi nanunso mwaona kuti anthu ambiri masiku ano akuvutika kuti agone mokwanira? [Yembekezani ayankhe.] Nkhaŵa kapena mavuto ndi zimene zingachititse vuto limeneli. [Ŵerengani Mlaliki 5:12.] Magazini iyi ikufotokoza zimene zimapangitsa kuti anthu azisoŵa tulo ndipo ili ndi mfundo zothandiza zimene tingachepetsere vuto la kusoŵa tulo.”

Nsanja ya Olonda May 1

“Mafunso ena anthu sangathe kuyankha. Monga funso ili. [Ŵerengani Yobu 21:7.] Kodi munayamba mwakhala ndi funso limene mumafuna kufunsa Mulungu? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza momwe anthu a m’madera onse a padziko lapansi apezera mayankho okhutiritsa a mafunso atatu ofunika kwambiri pamoyo.”

Galamukani! Apr. 8

“Kodi si zomvetsa chisoni kuti miyoyo ya achinyamata ambiri yawonongeka ndi mankhwala osokoneza bongo? [Yembekezani ayankhe.] Nthaŵi zambiri mavuto amayamba pamene achinyamata akuyanjana ndi anzawo oipa. [Ŵerengani 1 Akorinto 15:33.] Galamukani! iyi ikufotokoza zimene zimayambitsa achinyamata kugwiritsa ntchito mankhwala osokoneza bongo ndiponso zimene makolo angachite kuti ateteze ana awo.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena