Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 4/04 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 4/04 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Apr. 15

“Anthu ena amaganiza kuti zonse zimene zimachitika pamoyo wa munthu, kuphatikizapo masoka, chimakhala chifuniro cha Mulungu. Kodi munaganizapo zimenezi? [Yembekezani ayankhe.] Anthu ambiri amalidziŵa pemphero ili. [Ŵerengani Mateyu 6:10b.] Kodi chifuniro cha Mulungu polenga dziko lapansi n’chotani, ndipo kodi ndi liti pamene chidzakwaniritsidwe chonse? Magazini iyi ikupereka yankho la m’Baibulo.”

Galamukani! May 8

“Masiku ano, anthu ena amadziona kuti alibe chiyembekezo chilichonse. Kodi inuyo nthaŵi zina mumaonanso choncho? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Aroma 15:4.] Anthu ambiri amazindikira kufunika kokhala ndi chiyembekezo. Musangalala kuona zifukwa zisanu ndi ziŵiri za m’Malemba zokhalira ndi chiyembekezo zimene zili mu Galamukani! iyi.”

Nsanja ya Olonda May 1

“Poyesa kusintha anthu kuti akhale abwinopo, atsogoleri ena achipembedzo amaloŵerera m’ndale. Komabe, taonani zimene Yesu anachita anthu akufuna kumulonga ufumu. [Ŵerengani Yohane 6:15.] Yesu anaika mtima wake pachinthu chimene chikathandize ena kosatha. Magazini iyi ikufotokoza za chinthu chimenecho.”

Galamukani! May 8

“Anthu ambiri amakumana ndi mavuto kuntchito. Ena amavutitsidwa ndi anzawo akuntchito. Kodi mukudziŵa kuti Baibulo lili ndi malangizo amene angatithandize kulimbana ndi mavuto ngati amenewo? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Miyambo 15:1.] Magazini iyi ili ndi mfundo zothandiza pankhani ya zimene tingachite kuti tikhalebe pamtendere ndi ena kuntchito.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena