Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 12/03 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki wathu wa Ufumu—2002
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
km 12/03 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Dec. 15

“Panyengo ino ya pachaka, anthu ambiri amaganizira za kubadwa kwa Yesu. Kodi munayamba mwaganizirapo zoti anakulira m’banja lotani? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Luka 2:51, 52.] Magazini iyi ya Nsanja ya Olonda ikufotokoza maphunziro abwino omwe tingatolepo pankhani ya m’Baibulo ya mmene Yesu analeredwera.”

Galamukani! Dec. 8

“Anthu ena akuda nkhaŵa kuti dzikoli lawonongedwa moti silingakonzedwenso. Kodi inu mumaganiza kuti zinthu sizidzasintha? [Yembekezani ayankhe.] Cholinga cha Mlengi sichinali choti dzikoli lidzakhale dzala loti anthu sangakhalemo. [Ŵerengani Yesaya 45:18.] Magazini iyi ikulongosola mmene dzikoli lidzapulumutsidwire.”

Nsanja ya Olonda Jan. 1

“Anthu ambiri amalakalaka padziko pano patakhala mtendere. Kodi mukuganiza kuti nthaŵi ina tidzaona mawu aŵa atakwaniritsidwa? [Ŵerengani Salmo 46:9. Ndiyeno yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ya Nsanja ya Olonda ikufotokoza mmene zimenezi zidzakwaniritsidwire ndiponso chifukwa chomwe tingakhulupirire lonjezo la Mulungu lakuti padziko lapansi sipadzakhala nkhondo.”

Galamukani! Dec. 8

“Kodi mumaganiza kuti anthu adzakhala ndi moyo ngati uwu wofotokozedwa apa? [Ŵerengani Yesaya 14:7. Kenako yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ili ndi mfundo zabwino kwambiri zomwe tingapindule nazo pamene tikuyembekezera kukwaniritsidwa kwa malonjezo a Mulungu.” Sonyezani nkhani yakuti “Kodi Mungalimbane Bwanji ndi Zilakolako Zoipa?”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena