Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 2/04 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
km 2/04 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Feb. 15

“Anthu ambiri amavutika maganizo chifukwa cha zoipa zimene zachitidwa m’dzina la chipembedzo. Ambiri akuganiza kuti chipembedzo n’chimene chikuchititsa mavuto a anthu. Kodi munaganizapo zimenezi? [Yembekezani ayankhe. Kenako ŵerengani Chivumbulutso 18:24.] Magazini iyi ikufotokoza zimene Baibulo limanena pankhani imeneyi.”

Galamukani! Feb. 8

“Dzina lenileni la Mulungu limaoneka chonchi m’chinenero cha Chihebri. [M’sonyezeni pachikuto.] Anthu ena amakhulupirira kuti dzinali lisamatchulidwe. Ena amalitchulatchula. Galamukani! iyi ikufotokoza za nkhani imeneyi. Ikufotokozanso mmene tingadziŵire dzina la Mulungu.” Ŵerengani Salmo 83:18.

Nsanja ya Olonda Mar. 1

“Nthaŵi ina, Yesu Kristu anafunsidwa kuti: ‘Lamulo la m’tsogolo la onse ndi liti?’ Onani yankho lake. [Ŵerengani Marko 12:29, 30.] Kodi munadzifunsapo kuti Yesu anali kutanthauza chiyani? [Yembekezani ayankhe.] Nkhani yakuti ‘Mmene Timasonyezera Kuti Timakonda Mulungu’ ikufotokoza tanthauzo la mawu odziŵika kwambiri ameneŵa.”

Galamukani! Feb. 8

“Anthu ambiri masiku ano amagwira ntchito kwambiri ndipo amafunika kupuma mokwanira. Mwina mungavomereze mawu aŵa amene analembedwa zaka zoposa 3,000 zapitazo. [Ŵerengani Mlaliki 4:6. Ndiyeno m’loleni akambepo.] Galamukani! iyi ili ndi mfundo zothandiza za momwe tingadziŵire kuti tili ndi vuto la kusagona mokwanira ndiponso mmene tingathetsere vutolo.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena