Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 2/05 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
km 2/05 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda Feb. 15

“Nthawi zina, timamva nkhani zonena kuti kwachitika chozizwitsa. [Tchulani chitsanzo.] Anthu ena amakhulupirira nkhani zimenezi. Pamene ena amakayikira. Magazini iyi ikufotokoza ngati zozizwitsa zimene zili m’Baibulo zinachitikadi ndiponso ngati zinthu zimenezi zimachitikanso masiku ano.” Werengani Yeremiya 32:21.

Galamukani! Mar. 8

“Nthawi zakale, Mulungu analamula ana kulemekeza amayi awo ndiponso atate awo. [Werengani Eksodo 20:12.] Kodi muganiza kuti masiku ano amayi akulemekezedwa mmene afunikira? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza mavuto amene amayi akukumana nawo m’madera osiyanasiyana ndiponso zimene akuchita kuti athane ndi mavuto amenewo.”

Nsanja ya Olonda Mar. 1

“Kodi muganiza kuti dzikoli likanakhala malo abwino ngati aliyense akanagwiritsa ntchito langizo ili? [Werengani Aroma 12:17, 18. Ndiyeno yembekezani ayankhe.] N’zomvetsa chisoni kuti anthufe nthawi zina timasemphana maganizo. Magazini iyi ikusonyeza mmene kugwiritsira ntchito uphungu wa m’Baibulo kungatithandizire kuthetsa mikangano ndi kukhazikitsanso mtendere.”

Galamukani! Mar. 8

“Chiwerengero cha anthu ofuna magetsi chikukwera chaka chilichonse. Tangoganizani, n’chiyani chingachitike ngati titakhala tsiku limodzi opanda magetsi? [Yembekezani ayankhe.] Magazini iyi ikufotokoza kupita patsogolo komwe kwachitika kuti apeze gwero labwino la mphamvu za magetsi. Ikutchulanso za gwero la mphamvu zonse.” Werengani Yesaya 40:26.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena