Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 9/07 tsamba 1
  • Branch Letter

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Branch Letter
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Kuofesi ya Mboni za Yehova Kumachitika Zotani?
    Kodi Ndani Akuchita Chifuniro cha Yehova Masiku Ano?
  • Branch Letter
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Njira Zowonjezerera Utumiki Wanu
    Gulu Lochita Chifuniro cha Mulungu
  • Inali Yoyamba Zaka 100 Zapitazo
    Galamukani!—2001
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
km 9/07 tsamba 1

Branch Letter

Okondedwa Ofalitsa Ufumu Nonse:

Ndife osangalala kuona mmene ntchito ya Ufumu yapitira patsogolo m’gawo la nthambi yathu, m’chaka cha utumiki cha 2007. Ntchito yomanga Nyumba za Ufumu ndiponso Malo a Msonkhano yathandiza kuti tikhale ndi malo abwino olambirira amene amatamanda dzina la Yehova. Mungasangalale kudziwa kuti pofika kumapeto a mwezi wa May  2007, Nyumba za Ufumu 900 ndiponso Malo a Msonkhano 30 anali atamangidwa.

Amalizanso kumanga nyumba za Sukulu Yophunzitsa Utumiki, zimene zili pafupi ndi ofesi ya nthambi ku Lilongwe. Zinagwiritsidwa ntchito koyamba kuchitiramo Sukulu ya Oyang’anira Oyendayenda, imene inayamba pa February 2 ndipo inatha pa March 30, 2007. Nyumbazi zigwiritsidwanso ntchito kuchitiramo makalasi awiri oyambirira a Sukulu Yophunzitsa Utumiki omwe akhale m’Chingelezi, ndipo kenako makalasi otsatira adzakhala m’Chichewa.

Dziko la Malawi linali ndi chiwerengero chapamwamba chatsopano cha ofalitsa okwanira 68,611 m’mwezi wa April, 2007. Kameneka kanali kachiwiri m’chaka cha utumiki cha 2007 kukhala ndi chiwerengero chapamwamba chatsopano cha ofalitsa. Lipoti la April linasonyezanso chiwerengero chapamwamba chatsopano cha maphunziro a Baibulo chokwanira pafupifupi 73,000. Chiwerengerochi chikusonyeza kuti paavereji, wofalitsa aliyense anali ndi phunziro la Baibulo loposa limodzi.

Lipoti lomwe silinathe la chaka chino la anthu opezeka pa Chikumbutso okwanira 248,500 likusonyeza kuti chiwerengerochi chawonjezereka ndi anthu 60,000 kuposa chaka chatha. Ndipo zimenezi zikusonyeza kuti padakali ntchito yaikulu yopanga ophunzira. (Mateyo 28:19, 20) Ndife osangalala kugwira nanu limodzi ntchito yofunika imeneyi, ndipo landirani moni wathu wachikondi chachikhristu.

Ndife abale anu,

Ofesi ya Nthambi ya Malawi

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena