Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 11/09 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
km 11/09 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda November 1

“Zikuoneka kuti mabanja ambiri akukumana ndi zinthu zosautsa kwambiri. Kodi mukuganiza kuti n’chiyani chingachitikire mabanja ngati am’banjamo atamatsatira maganizo a Yesu awa? [Werengani Mateyo 20:28. Kenako dikirani ayankhe.] Nkhani iyi ikufotokoza zinthu zisanu zimene mabanja angaphunzire kwa Yesu.” Asonyezeni nkhani imene yayambira patsamba 16.

Galamukani! November

“Kodi mukuona kuti zipembedzo zimalimbikitsa kuti anthu azikondana ndiponso kukhala mwamtendere kapena kuti anthu azidana ndi kuchitirana chiwawa? [Yembekezerani ayankhe.] Zikuoneka kuti ambiri satsatira mawu a Yesu awa. [Werengani Mateyo 5:44, 45.] Nkhani iyi ikuyankha funso lakuti, Kodi n’zotheka munthu kukonda adani ake?” Asonyezeni nkhani imene yayambira patsamba 10.

Nsanja ya Olonda December 1

“Kodi mukuganiza kuti tsiku lina Mulungu angadzathetse mavuto padzikoli? [Yembekezerani ayankhe.] Lonjezo la m’Baibulo ili likutipatsa chifukwa choyembekezera zabwino. [Werengani lemba limodzi pa malemba amene ali m’bokosi patsamba 7.] Magazini iyi ikufotokoza zimene Baibulo limanena zokhudza nthawi ndiponso mmene Mulungu adzathetsere mavuto onse.”

Galamukani! December

“Ena amakhulupirira kuti zinthu za padzikoli ndi za kumwambaku zinachita kulengedwa, pamene enanso amati zinangokhalako zokha ndipo zilibe cholinga chenicheni. Kodi inuyo mukuganiza bwanji? [Yembekezerani ayankhe.] Taonani zimene Baibulo limanena. [Werengani Aheberi 3:4.] Magaziniyi ikufotokoza bwino kumene kunachokera zinthuzi ndiponso cholinga chake.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena