Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 5/10 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
km 5/10 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda May 1

“Kodi mukuganiza kuti zinthu zikanakhala bwino padzikoli munthu aliyense akanati azitsatira mawu a Yesu awa?” [Werengani Mateyo 7:12. Kenako yembekezerani ayankhe.] Nkhani iyi ikufotokoza zinthu zina zimene Yesu anaphunzitsa zimene zikusonyeza zinthu zomwe Mkhristu weniweni ayenera kuchita.” Asonyezeni nkhani imene yayambira patsamba 16.

Galamukani! May

“Kodi mukuganiza kuti mavuto a zachuma amene ali padzikoli atha posachedwapa? [Yembekezani ayankhe.] Anthu ambiri samadziwa mmene Baibulo lingatithandizire m’nthawi yovuta ino. [Werengani lemba limene lili m’nkhaniyi.] Nkhani iyi ikusonyeza mmene malangizo a m’Baibulo angatithandizire kupirira tikakumana ndi vuto la ndalama.” Asonyezeni nkhani imene yayambira patsamba 18.

Nsanja ya Olonda June 1

“Masiku ano m’matchalitchi ambiri samalalikira za uchimo kusiyana ndi mmene zinkakhalira m’mbuyomu. Kodi mumakhulupirira kuti nkhani ya uchimo ndi yachikalekale, kapena mumaona kuti ndi nkhani yofunika kuiganizira kwambiri? [Yembekezani ayankhe. Kenako werengani Aroma 5:12.] Magazini iyi ikufotokoza zimene Baibulo limanena pa nkhani ya uchimo.”

Galamukani! June

“Anthu ena akuona kuti zinthu zopanikiza zikuchulukirachulukirabe. Kodi mukuona kuti zimenezi ndi zoona? [Yembekezani ayankhe.] Anthu ambiri amaona kuti chifukwa chimodzi chimene chikuchititsa kuti tizikhala opanikizika kwambiri ndi ichi. [Werengani 2 Timoteyo 3:1.] Magazini iyi ikufotokoza mmene zinthu zopanikiza zimakhudzira moyo wathu. Ikufotokozanso mfundo zina zimene zingatithandize kuti tisamakhale opanikizika kwambiri.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena