Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 11/10 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
km 11/10 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogawira Magazini

Nsanja ya Olonda November 1

“Kodi mumaganiza kuti angelo amachita chidwi ndi zochita zathu? [Yembekezani ayankhe.] Baibulo limanena mfundo yochititsa chidwi iyi. [Werengani Luka 15:10.] Magazini iyi ikufotokoza zimene Yesu ananena zokhudza zolengedwa zauzimu komanso mmene zochita zawo zimatikhudzira.” Kenako, muonetseni nkhani imene ikuyambira patsamba 16.

Galamukani! November

Werengani 2 Timoteyo 3:16. Kenako funsani kuti: “Kodi inuyo mumaona kuti tiyenera kukhulupirira chilichonse chimene Baibulo limanena? [Yembekezani ayankhe.] Zimene nkhani iyi ikufotokoza zikusonyeza kuti zimene mbiri ya zinthu zakale zokumbidwa pansi ndi mabuku a mbiri yakale amanena zimagwirizana ndi zimene Baibulo limanena zokhudza dziko lakale la Iguputo.” Kenako, muonetseni nkhani imene ikuyambira patsamba 15.

Nsanja ya Olonda December 1

“Anthu ambiri amakhulupirira kuti kumalo amizimu kuli mizimu imene imalamulira zochita zathu. Kodi inu mukuganiza bwanji? [Yembekezani ayankhe. Kenako werengani Chivumbulutso 12:7-9.] Magazini iyi ikufotokoza zimene Baibulo limanena zokhudza amene amakhala ku malo amizimu, mmene zochita zawo zimatikhudzira komanso ngati zili zotheka kulankhulana nawo.”

Galamukani! December

“Kodi munayamba mwaganizapo kuti ndi chifukwa chiyani anthu amakondwerera Khirisimasi pa 25 December ngakhale kuti Baibulo silinena tsiku limene Yesu anabadwa? [Yembekezani ayankhe.] Zomwe vesi ili likufotokoza zikusonyeza kuti sizingatheke kuti Yesu anabadwa m’nyengo imeneyi yomwe imakhala nyengo yozizira kumadera a kumpoto kwa dziko lapansili. [Werengani Luka 2:8.] Magazini iyi ikufotokoza chiyambi cha miyambo ina yotchuka imene imachitika nthawi ya Khirisimasi.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena