Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 9/13 tsamba 3
  • Amenewanso Muziwaganizira

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Amenewanso Muziwaganizira
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Nkhani Yofanana
  • Tiziphunzira kwa Ofalitsa Aluso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Mmene Mungaphunzitsire Ofalitsa Atsopano Kulalikira
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Kuwonjezera Luso Lathu mu Utumiki—Muziphunzitsa Ofalitsa Atsopano
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Chitani Changu pa Zinthu Zabwino!
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
km 9/13 tsamba 3

Amenewanso Muziwaganizira

M’mipingo yambiri muli ofalitsa amene sangathe kuchita zambiri mu utumiki chifukwa cha matenda kapena ukalamba. (2 Akor. 4:16) Ndiye kodi mungapempheko ofalitsa amenewa kuti azikhala nanu mukamachititsa phunziro la Baibulo? Ngati wofalitsayo ali woti sangathe kuchoka pakhomo, mwina mungachite bwino kupita ndi wophunzira wanu kunyumba kwa wofalitsayo n’kukaphunzirira komweko. Komanso nthawi zina mungatenge wofalitsa yemwe amalephera kuchita zambiri mu utumiki chifukwa cha matenda kuti mukalalikire naye limodzi khomo ndi khomo nyumba zochepa kapena kupita naye ku ulendo wobwereza. Mungapite naye kwa munthu mmodzi kapena awiri. Ofalitsa achikulire ambiri amakhala aluso mu utumiki, choncho kuchita zimenezi sikungowaganizira iwowo, koma inunso mudzapindula kwambiri. (Aroma 1:12) Kuwonjezera pamenepo, mukamayesetsa kusonyeza chikondi kwa ena m’njira imeneyi, Yehova adzakudalitsani.—Miy. 19:17; 1 Yoh. 3:17, 18.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena