Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 March tsamba 4
  • Yobu Anakhalabe Wokhulupirika Pamene Ankayesedwa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yobu Anakhalabe Wokhulupirika Pamene Ankayesedwa
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Yobu Analemekeza Dzina la Yehova
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Yobu Anapitiriza Kutumikira Mulungu ndi Mtima Wosagawanika
    Kodi Baibulo Lili Ndi Uthenga Wotani?
  • Mfundo Zazikulu za M’buku la Yobu
    Nsanja ya Olonda—2006
  • Pitirizani Kukhala ndi Mtima Wosagawanika
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2019
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 March tsamba 4

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | YOBU 1-5

Yobu Anakhalabe Wokhulupirika Pamene Ankayesedwa

Satana akuyang’ana Yobu

Yobu ankakhala m’dziko la Uzi pa nthawi imene Aisiraeli anali akapolo ku Iguputo. Ngakhale kuti sanali Mwisiraeli, iye ankalambira Yehova. Anali ndi banja lalikulu ndipo anali wolemera kwambiri. Iye anali munthu wolemekezeka, ankaweruza milandu mwachilungamo komanso ankathandiza anthu osauka. Yobu anali wokhulupirika kwa Mulungu.

Zimene Yobu anachita zinasonyeza kuti ankakonda kwambiri Yehova

1:8-11, 22; 2:2-5

  • Satana ankadziwa kuti Yobu ndi munthu wokhulupirika. Iye sanakane zoti Yobu ankamvera Yehova, koma anakayikira ngati ankatumikira Yehova ndi zolinga zabwino

  • Satana ananena kuti Yobu ankatumikira Yehova chifukwa cha zinthu zabwino zimene ankamuchitira

  • Pofuna kutsimikizira kuti zimene ankanenazo zinali zabodza, Yehova analola Satana kuti ayese Yobu. Choncho, Satana anachititsa kuti Yobu akumane ndi mavuto ambiri pamoyo wake

  • Ngakhale kuti Yobu anapitiriza kukhala wokhulupirika kwa Yehova, Satana anayamba kukayikira ngati anthu angamatumikire Mulungu mokhulupirika pamene akukumana ndi mavuto

  • Yobu sanachimwe kapena kunena kuti Mulungu amachita zoipa

Yobu wathedwa nzeru
    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena