Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb17 July tsamba 8
  • Tizisonyeza Ulemu Tikafika Pakhomo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Tizisonyeza Ulemu Tikafika Pakhomo
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
  • Nkhani Yofanana
  • Chititsani Maphunziro a Baibulo Achidule Ndiponso a Patelefoni Opita Patsogolo
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • “Mayendedwe Anu Ayenere Uthenga Wabwino”
    Nsanja ya Olonda—1989
  • Kulimirira Mayendedwe Achikristu M’dziko Lopanda Mayendedwe
    Nsanja ya Olonda—1989
  • Kuwonjezera Luso Lathu mu Utumiki—Kuyambitsa Phunziro Lachidule Pogwiritsa Ntchito Kabuku ka Uthenga Wabwino Wochokera kwa Mulungu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
mwb17 July tsamba 8

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Tizisonyeza Ulemu Tikafika Pakhomo

Abale ali mu utumiki ndipo pamene afika pakhomo, m’bale wina akusunzumira pawindo, akudya komanso wina akulemba meseji

Akhristufe tili ngati “choonetsedwa m’bwalo la masewera kudziko.” (1 Akor. 4:9) N’chifukwa chake sitiyenera kudabwa kuti anthu ena amatisunzumira pawindo kapena kutimvetsera ali m’nyumba zawo. Nyumba zina zimakhala ndi makamera omwe amathandiza kuti eninyumba aziona, kumva ndiponso mwina kujambula zimene tikulankhula. Ndiye tiyeni tione njira zina zimene tingasonyezere ulemu tikafika pakhomo la munthu amene tikufuna kumulalikira.​—2 Akor. 6:3.

KHALIDWE LANU (Afil. 1:27):

  • Mungasonyeze ulemu kwa eninyumba popewa kusunzumira m’nyumba zawo. Simuyeneranso kudya, kumwa, kulankhula pafoni kapena kulemba mameseji mukafika pakhomo la munthu

ZOLANKHULA ZANU (Aef. 4:29):

  • Mukafika pakhomo, musamalankhule zilizonse zimene sizingasangalatse mwininyumbayo. Ofalitsa ena amasankha kusiya kaye kulankhulana n’cholinga choti aziganizira zimene akufuna kukambirana ndi mwininyumbayo

Abale awiri aima mwaulemu pakhomo pamene mwininyumba akuwasunzumira

Kodi ndi njira zinanso ziti zimene mungasonyezere ulemu mukafika pakhomo pamene muli mu utumiki?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena