Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb18 February tsamba 4
  • “Uzilemekeza Bambo Ako ndi Mayi Ako”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • “Uzilemekeza Bambo Ako ndi Mayi Ako”
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
  • Nkhani Yofanana
  • Chitirani Ulemu Anthu Onse
    Nsanja ya Olonda—1991
  • Kulemekeza Makolo Athu Okalamba
    Chinsinsi cha Chimwemwe cha Banja
  • Kodi Munthu Angasonyeze Bwanji Kuti ‘Amalemekeza Bambo Ake ndi Mayi Ake’?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Lemekezani Yehova—Chifukwa Ninji Ndipo Motani?
    Nsanja ya Olonda—1991
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
mwb18 February tsamba 4

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

“Uzilemekeza Bambo Ako ndi Mayi Ako”

Pamene Yesu anali padzikoli, anauza anthu lamulo lakuti: “Uzilemekeza bambo ako ndi mayi ako.” (Eks. 20:12; Mat. 15:4) Yesu anali ndi ufulu wolankhula pa nkhaniyi chifukwa iye ali mwana ‘anapitiriza kumvera’ makolo ake. (Luka 2:51) Atakula, anakonza zoti mayi ake asamaliridwe bwino iyeyo akamwalira.​—Yoh. 19:26, 27.

Masiku anonso, achinyamata achikhristu omwe amamvera makolo awo komanso kulankhula nawo mwaulemu, amasonyeza kuti amawalemekeza. Lamulo loti tizilemekeza makolo athu limagwirabe ntchito ngakhale makolowo atakalamba. Tingasonyeze kuti timawalemekezabe tikamafunsira nzeru kwa iwo. (Miy. 23:22) Timalemekezanso makolo athu okalamba tikamawasamalira ndi kuwapatsa zofunika pa moyo wawo ngati pakufunika kutero. (1 Tim. 5:8) Kaya ndife achichepere kapena achikulire, kuyesetsa kulankhulana ndi makolo athu kungatithandize kuti tiziwalemekeza.

ONERANI VIDIYO YAKUTI KODI NDINGATANI KUTI NDIZILANKHULANA BWINO NDI MAKOLO ANGA? KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • N’chifukwa chiyani nthawi zina zingakhale zovuta kulankhulana ndi makolo anu?

  • Kodi mungalemekeze bwanji makolo anu mukamalankhula nawo?

    Mnyamata akulembera makolo ake kalata, akuyankhula ndi makolo ake komanso akusewera mpira ndi bambo ake
  • N’chifukwa chiyani muyenera kuyesetsa kuti muzilankhula ndi makolo anu? (Miy. 15:22)

    Makolo akuthandiza mwana kuti adzalimbane ndi mavuto amene angadzakumane nawo

    Kulankhulana ndi makolo anu kungathandize kuti zinthu zizikuyenderani bwino

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena