Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb20 February tsamba 7
  • Kodi Mumapindula ndi Kabuku ka Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mumapindula ndi Kabuku ka Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku?
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
  • Nkhani Yofanana
  • Ndandanda ya Banja Yochitira Lemba la Tsiku
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Mitu ya Mabanja—Khalanibe ndi Ndandanda Yabwino Yochitira Zinthu Zauzimu
    Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Kulozera Maganizo a Omvetsera ku Baibulo
    Buku Lolangiza la Sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Konzani Ndandanda ya Banja Yotheka Kuitsatira
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
mwb20 February tsamba 7

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Kodi Mumapindula ndi Kabuku ka Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku?

Kodi muli ndi pulogalamu yowerenga lemba ndi ndemanga kuchokera m’kabuku ka Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku? Ngati sichoncho, muyenera kuyesetsa kumachita zimenezi. Ambiri amasankha kupanga lemba la tsiku m’mawa. Zimenezi zimathandiza kuti aziganizira mfundo za lembalo tsiku lonse. (Yos. 1:8; Sal. 119:97) Kodi mungatani kuti muzipindula kwambiri ndi lemba la tsiku? Mungachite bwino kuwerenga vesilo m’Baibulo kuti mumvetse nkhani yake. Ganizirani nkhani ya m’Baibulo yomwe ikufotokoza bwino mfundo ya mulembalo. Kenako onani mmene mungaigwiritsire ntchito. Mukamalola kuti mawu a Mulungu azikutsogolerani posankha zochita, mudzapindula kwambiri.​—Sal. 119:105.

Anthu otumikira pa Beteli padziko lonse amakambirana lemba la tsiku pa nthawi ya chakudya cham’mawa. Zaka zaposachedwapa, zambiri mwa mfundo zimene amakambirana pa lemba la tsiku zakhala zikuikidwa pa JW Broadcasting,® pambali yakuti MAPULOGALAMU KOMANSO ZOCHITIKA ZINA. Kodi ndi liti limene munaonera imodzi mwa mapulogalamu amenewa? Nkhani zake zingakulimbikitseni kwambiri. Mwachitsanzo, kodi nkhani ya Loti ingakuthandizeni bwanji posankha zochita?

ONERANI VIDIYO YAKUTI MUSAMAKONDE DZIKO (1 YOH. 2:15), KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi ndi mfundo ya m’Baibulo iti imene inali maziko a kukambirana pa kulambira kwa m’mawa kumeneku?

  • Kodi nkhani ya Loti ikutithandiza bwanji kuona kuopsa kokonda dziko kapena zinthu za m’dzikoli?​—Gen. 13:12; 14:12; 19:3, 12, 13, 24-26

  • Kodi tingasonyeze bwanji kuti timakonda Yehova osati dziko kapena zinthu za m’dziko?

Zithunzi: M’bale akuganizira zimene wawerenga m’kabuku ka Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku kwa tsiku lonse. 1. M’bale akuwerenga lemba la tsiku ndipo akuyerekezera kuti akuona angelo akutulutsa Loti ndi banja lake mumzinda wa Sodomu. 2. M’bale akudya pamene akupuma kuntchito ndipo akupitirizabe kuganizira zimene anawerenga m’mawa pa lemba la tsiku. 3. M’bale ali kunyumba madzulo ndipo akupitirizabe kuganizira zokhudza zimene anawerenga pa lemba la tsiku m’mawa kwinaku akupinda zovala.

Kodi ndingasonyeze bwanji kuti ndimaona Mawu a Mulungu kukhala ofunika pa zochita zanga za tsiku lonse?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena