Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 5/05 tsamba 3-6
  • Konzani Ndandanda ya Banja Yotheka Kuitsatira

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Konzani Ndandanda ya Banja Yotheka Kuitsatira
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Nkhani Yofanana
  • Ndandanda ya Banja Yochitira Lemba la Tsiku
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Mangani Moyo Wanu pa Utumiki wa Yehova
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
  • Mmene Banja Limachitira Zinthu Kuti Onse Azitengamo Mbali Mokwanira—Pa Phunziro la Baibulo
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
  • Musafulumire Kuganiza Kuti Simungakwanitse—Zimene Mungachite Ngati Muli Wotanganidwa
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2012
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
km 5/05 tsamba 3-6

Konzani Ndandanda ya Banja Yotheka Kuitsatira

1 Pa Ulaliki wake wa pa Phiri, Yesu analimbikitsa omvera ake kuti: ‘Koma muthange mwafuna Ufumu wake ndi chilungamo chake.’ (Mat. 6:33) Njira yabwino yokonzera zochita za banja kuti muike zinthu zauzimu patsogolo ndiyo kukhala ndi ndandanda yochita kulemba. Pezani nthawi yoti mukonze ndandanda ya banja lanu ya mlungu ndi mlungu pogwiritsa ntchito ndandanda yosamaliza yomwe ili patsamba 6 m’mphatika ino. Mabanja ena angakonde kungodula zimene talembazo n’kuzimata pa ndandandayo. Ena angasankhe kuchita kulemba okha zofunika kuchitazo.

2 Chitsanzo cha ndandanda ili m’munsiyi chingakuthandizeni pamene mukukonza ndandanda yanu ya banja. Muona kuti ili ndi zochita zinayi zofunika: (1) Kupezeka pa misonkhano ya mpingo, (2) utumiki wa kumunda wa banja, (3) phunziro la banja, ndipo (4) kukambirana lemba la tsiku. Kuphatikiza zinthu zimenezi pa ndandanda yanu kungakuthandizeni kuti “mutsimikizire zinthu zofunika kwambiri.” (Afil. 1:10, NW) Mfundo zina zokhudza mbali zinayi zimenezi zili patsamba 4 ndi 5.

3 Sikuti ndandanda ya banja lanu ingokhala ndi zochita zinayi zokhazi ayi. Ngati mumakonzekera misonkhano ina monga banja, lembani zimenezo pa ndandanda yanuyo. Ngati mumawerenga kachigawo ka Baibulo nonse pamodzi mukatha kukambirana lemba la tsiku kapena mumachita zimenezi panthawi ina, zilembeni pa ndandanda yanu. Ngati muli ndi chizolowezi chosewera monga banja, zimenezi mungaziphatikize pa ndandanda yanu.

4 Ndandanda yanu ya banja ikhale yogwirizana ndi zosowa za aliyense m’banja ndi zochita zake. Pakapita nthawi, muziona kuti ikuyenda bwanji, ndipo muziisintha ngati pali kufunikira kotero.

[Tchati patsamba 3]

Chitsanzo cha Ndandanda ya Banja

M’mawa Masana Madzulo

Laml. Lemba la Tsiku

Nkhani ya Onse ndi

Phunziro la Nsanja ya Olonda

Lole. Lemba la Tsiku Phunziro la Banja

Lachiw. Lemba la Tsiku Phunziro la Buku

la Mpingo

Lachit. Lemba la Tsiku

Lachin. Lemba la Tsiku Sukulu ya Utumiki

wa Mulungu ndi

Msonkhano wa

Utumiki

Lachis. Lemba la Tsiku

Low. Lemba la Tsiku

Utumiki wa Kumunda

wa Banja

(Tsiku la Magazini)

[Tchati patsamba 6]

Ndandanda ya Banja

M’mawa Masana Madzulo

Laml.

Lole.

Lachiw.

Lachit.

Lachin.

Lachis.

Low.

..................................................................

Lemba la Lemba la Lemba la Lemba la Lemba la Lemba la Lemba la

Tsiku Tsiku Tsiku Tsiku Tsiku Tsiku Tsiku

Nkhani Sukulu Phunziro Phunziro Utumiki Kuwerenga Kusewera

ya Onse ya la Buku la Banja wa Kumunda Baibulo Monga

ndi Utumiki wa la Monga Banja Monga Banja Banja

Phunziro Mulungu ndi Mpingo

la Nsanja Msonkhano

ya Olonda wa

Utumiki

Mwina mungakonde kupanga fotokope tsamba lino la Utumiki Wathu wa Ufumu n’kuduladula bwinobwino mmene muli mizera ya madonthomadonthomo. Mukatero mukhoza kumata timapepala mwadulato pa ndandanda yosalembapo chilichonse imene ili panoyi mogwirizana ndi zochita za banja lanu za mlungu ndi mlungu. Malo osalembawo m’mizera ya madonthomadontho, mukhoza kuwagwiritsa ntchito kulembamo zochita zina zimene mungafune kuziphatikiza pandandanda yanu ya mlungu ndi mlungu.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena