Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb22 May tsamba 7
  • Kodi Mwakonzeka Kukumana Ndi Zachiwawa?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi Mwakonzeka Kukumana Ndi Zachiwawa?
  • Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Mwakonzekera?
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
  • Khalanibe Okonzeka Pamene Tili Kumapeto kwa “Masiku Otsiriza”
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
  • Kodi Mwakonzeka Kukumana ndi Mavuto Azachuma?
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Kuwonjezera Luso Lathu mu Utumiki​—Muzithandiza Ophunzira Anu Kuti Azikonzekera
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
Onani Zambiri
Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
mwb22 May tsamba 7
Banja likuonera pa TV nkhani zokhudza chiwawa zimene zikuchitika. Pafupi pawo pali zikwama zomwe muli zinthu zomwe angatenge ngati patachitika ngozi zadzidzidzi.

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Kodi Mwakonzeka Kukumana ndi Zachiwawa?

Pamene mapeto a dzikoli akuyandikira, zachiwawa, uchigawenga komanso nkhondo ziziwonjezerekabe. (Chv 6:4) Kodi tingakonzekere bwanji mavutowa panopa?

  • Muzikonzekera mwauzimu: Fufuzani mfundo komanso nkhani za m’Baibulo zomwe zingakuthandizeni kuti muzikhulupirira kwambiri Yehova ndi gulu lake komanso kuti musakhale mbali ya dziko. (Miy 12:5; jr 125-126 ¶23-24) Ino ndiyo nthawi yoti tikhale pa ubwenzi wolimba ndi abale ndi alongo mumpingo.​—1Pe 4:7, 8

  • Muzikonzekera mwakuthupi: Muzidziwiratu malo amene mungakakhaleko motetezeka komanso zinthu zofunika zokwanira ndipo muzikonzekereratu mmene mungachokere panyumba. Muzionanso zimene munasunga mu chikwama chanu chomwe mumaikamo zinthu zofunika zomwe mungatenge ngati patachitika ngozi zadzidzidzi, kuphatikizapo ndalama komanso zinthu zodzitetezera ku matenda monga magulovesi ndi masiki. Muzidziwa mmene mungalumukizirane ndi akulu ndipo muzionetsetsa kuti ali ndi nambala yanu ya foni.​—Yes 32:2; g17.5 3-7

Kukamachitika zipolowe, muzionetsetsa kuti mukupitirizabe kuchita zinthu zomwe mumachita polambira Yehova monga kupemphera, kuphunzira panokha komanso kupezeka pamisonkhano. (Afi 1:10) Musamayendeyende kupatulapo ngati pakufunika kutero. (Mt 10:16) Muzigawana zakudya komanso zinthu zina.​—Aro 12:13.

ONERANI VIDIYO YAKUTI KODI MWAKONZEKA KUKUMANA NDI NGOZI ZOGWA MWADZIDZIDZI?, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi Yehova angatithandize bwanji pa nthawi imene kwachitika ngozi zadzidzidzi?

  • Kodi tingakonzekere bwanji?

  • Kodi tingathandize bwanji anthu ena amene akhudzidwa ndi ngozizi?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena