Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb23 September tsamba 15
  • Makolo, Muzithandiza Ana Anu Kupeza Nzeru Zochokera kwa Mulungu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Makolo, Muzithandiza Ana Anu Kupeza Nzeru Zochokera kwa Mulungu
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Nkhani Yofanana
  • Muzigwiritsa Ntchito Mfundo za M’Baibulo Pothandiza Ana Anu Kuti Zinthu Ziwayendere Bwino
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Zosankha Zomwe Zimasonyeza Kuti Timadalira Yehova
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • ‘Anthu a Maganizo Abwino’ Adzamvetsera
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
  • Muziwerenga Baibulo Tsiku Lililonse Komanso Muzifunafuna Nzeru
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
mwb23 September tsamba 15
Mlongo akuthandiza ana ake kuti aziyankha komanso azitsatira pa misonkhano.

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Makolo, Muzithandiza Ana Anu Kupeza Nzeru Zochokera kwa Mulungu

Njira imodzi imene makolo angathandizire ana awo kupeza nzeru zochokera kwa Mulungu, ndi kuwathandiza kuti azipindula ndi misonkhano ya Chikhristu. Zomwe ana amaona, kumva komanso kufotokoza mu ndemanga zimene amapereka pamisonkhano zimawathandiza kudziwa zokhudza Yehova komanso kukhala anzake apamtima. (De 31:​12, 13) Ngati ndinu kholo, kodi mungathandize bwanji mwana wanu kuti azipindula kwambiri ndi misonkhano?

  • Muziyesetsa kupezeka pa misonkhano ya mpingo pamasom’pamaso ku Nyumba ya Ufumu.—Sl 22:22

  • Muzikhala ndi nthawi yokwanira yocheza ndi abale ndi alongo pa Nyumba ya Ufumu misonkhano isanayambe kapena ikatha.—Ahe 10:25

  • Muzionetsetsa kuti aliyense m’banja lanu ali ndi mabuku kapena magazini ophunzirira pamisonkhano, kaya a pazipangizo zamakono kapena osindikizidwa

  • Muzithandiza mwana wanu kukonzekera kukapereka ndemanga m’mawu akeake.—Mt 21:​15, 16

  • Muzilankhula zinthu zabwino zokhudza misonkhano komanso zimene timaphunzirako

  • Muzithandiza ana anu kuti azichita nawo zinthu zosiyanasiyana monga kuyeretsa pa Nyumba ya Ufumu kapena kucheza ndi abale ndi alongo achikulire a mumpingo mwanu

Kuthandiza ana anu kuti akhale pa ubwenzi wolimba ndi Yehova kumafuna khama, ndipo nthawi zina kungaoneke ngati kovuta kwambiri. Komabe mukhoza kukhala otsimikiza kuti Yehova akuthandizani.—Yes 40:29.

ONERANI VIDIYO YAKUTI MAKOLO, MUZIDALIRA YEHOVA KUTI AZIKUPATSANI MPHAMVU, KENAKO YANKHANI MAFUNSO OTSATIRAWA:

  • Kodi kutopa chifukwa chosamalira mwana, kunakhudza bwanji Zack ndi Leah?

  • N’chifukwa chiyani makolo ayenera kudalira Yehova kuti awapatse mphamvu?

  • Kodi Zack ndi Leah anasonyeza bwanji kuti amadalira Yehova kuti awathandize?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena