Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • wp21 No. 3 tsamba 3
  • Aliyense Amafuna Kukhala Ndi Tsogolo Labwino

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Aliyense Amafuna Kukhala Ndi Tsogolo Labwino
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2021
  • Nkhani Yofanana
  • Mawu Oyamba
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2021
  • N’zotheka Kukhala Ndi Tsogolo Labwino
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2021
  • Kodi Kungokhala Munthu Wabwino N’kumene Kungachititse Kuti Tikhale Ndi Tsogolo Labwino?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2021
  • Kodi Maphunziro Ndi Ndalama Zingatithandize Kukhala Ndi Tsogolo Labwino?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2021
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2021
wp21 No. 3 tsamba 3
Makolo ali ndi mwana wawo wamkazi ndipo akuyang’ana maluwa omwe aphukira mumtengo.

Aliyense Amafuna Kukhala Ndi Tsogolo Labwino

Kodi inuyo mumafuna kukhala ndi tsogolo lotani? Mofanana ndi anthu ambiri, sitikukayikira kuti inunso mumafuna kukhala ndi tsogolo labwino limodzi ndi banja lanu. Mumafuna mutakhala osangalala, athanzi, kukhala moyo wamtendere komanso wosasowa chilichonse.

Komabe, anthu ambiri amakayikira kuti angakhale ndi tsogolo labwino. Mwachitsanzo, mliri wa COVID-19, womwe anthu sankauyembekezera, wakhudza miyoyo ya anthu ambiri, wayambitsa umphawi ngakhalenso kupha anthu ambirimbiri. Chifukwa cha zimenezi, anthu ambiri amaona kuti n’zosatheka kukhala ndi tsogolo labwino.

Popeza kuti sakudziwa zokhudza tsogolo lawo, anthu akufunafuna zinthu zimene zingawathandize kuti akhale ndi tsogolo labwino. Ena amakhulupirira kuti pali mphamvu zinazake zosaoneka zimene zingathe kuwabweretsera tsoka kapena mwayi pa moyo wawo. Anthu ambiri amaganiza kuti maphunziro ndi chuma, ndi zimene zingawathandize kuti adzakhale ndi tsogolo labwino. Pomwe ena amaona kuti akungofunika kukhala munthu wabwino n’cholinga choti akhale ndi moyo wabwino.

Kodi zinthu zimenezi zingakuthandizenidi kukhala ndi tsogolo labwino? Kuti mudziwe zoona zake, ganizirani mafunso awa:

  • Kodi tsogolo lanu mungalidziwe bwanji?

  • Kodi maphunziro ndi ndalama, n’zimene zingatithandize kukhala ndi moyo wabwino?

  • Kodi kungokhala munthu wabwino n’kumene kungachititse kuti mukhale ndi tsogolo labwino?

  • Kodi mungapeze kuti malangizo odalirika omwe angakuthandizeni kukhala ndi tsogolo labwino?

Magaziniyi ikuthandizani kupeza mayankho a mafunso amenewa.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena