-
Esitere 8:9Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
9 Choncho anaitana alembi+ a mfumu pa nthawi imeneyo, m’mwezi wachitatu umene ndi mwezi wa Sivani,* pa tsiku la 23 la mweziwo. Iwo analemba makalatawo mogwirizana ndi zimene Moredekai ananena. Makalatawo anali opita kwa Ayuda, masatarapi,*+ abwanamkubwa ndi akalonga a m’zigawo zonse kuchokera ku Indiya kukafika ku Itiyopiya, zigawo 127.+ Chigawo chilichonse anachilembera makalata amenewa malinga ndi mmene anthu a m’chigawocho anali kulembera+ ndiponso m’chinenero chawo.+ Nawonso Ayuda anawalembera malinga ndi mmene iwo anali kulembera ndiponso m’chinenero chawo.+
-