Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
  • Lero

Loweruka, July 19

Nthawi indichepera kuti ndipitirize kufotokoza za Gidiyoni.—Aheb. 11:32.

Gidiyoni anayankha modekha pamene amuna a ku Efuraimu ankamuimba mlandu. (Ower. 8:1-3) Iye sanayankhe mokwiya. Iye anasonyeza kuti anali wodzichepetsa powamvetsera komanso kulankhula nawo mokoma mtima, zomwe zinachititsa kuti mitima ya anthuwo ikhale m’malo. Akulu anzeru amatsanzira Gidiyoni pomvetsera mosamala komanso kuyankha modekha akamaimbidwa mlandu. (Yak. 3:13) Akamachita zimenezi amathandiza kuti mumpingo mukhale mtendere. Pamene anthu anayamba kutamanda Gidiyoni chifukwa chopambana pankhondo yolimbana ndi Amidiyani, iye anathandiza anthuwo kuti apereke ulemerero kwa Yehova. (Ower. 8:22, 23) Kodi abale audindo angatsanzire bwanji Gidiyoni? Iwo ayenera kupereka ulemerero kwa Yehova chifukwa cha zimene akwanitsa kuchita. (1 Akor. 4:6, 7) Mwachitsanzo, ngati mkulu akutamandidwa chifukwa cha luso lophunzitsa lomwe ali nalo, iye angathandize anthuwo kuti aziganizira kumene kukuchokera mfundo zomwe amaphunzitsazo, komwe ndi m’Mawu a Mulungu, kapena maphunziro omwe gulu la Yehova limapereka. Nthawi ndi nthawi, akulu ayenera kumadzifufuza kuti aone ngati akuchititsa anthu kuti azitamanda iwowo m’malo mwa Yehova. w23.06 4 ¶7-8

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025

Lamlungu, July 20

Maganizo anga ndi osiyana ndi maganizo anu.​—Yes. 55:8.

Ngati zimene tapempha sizikuchitika tiyenera kudzifunsa kuti, ‘Kodi zimene ndikupemphazi ndi zoyenera?’ Nthawi zambiri anthu timaganiza kuti timadziwa zomwe ndi zoyenera kwa ifeyo. Koma zomwe timapempha zikhoza kukhala zosathandiza kwenikweni. Tikamapempherera vuto linalake, pakhoza kukhala njira ina yabwino yothetsera vutolo kusiyana ndi imene tikupempha. Ndipo zinthu zina zomwe tingapemphe zingakhale zosagwirizana ndi zimene Yehova amafuna. (1 Yoh. 5:14) Mwachitsanzo, taganizirani za makolo omwe anapempha Yehova kuti mwana wawo apitirizebe kukhala m’choonadi. Zimene anapemphazi zikhoza kuoneka ngati zoyenera. Koma Yehova sakakamiza munthu aliyense kuti azimutumikira. Amafuna kuti aliyense azisankha kumutumikira, ngakhalenso ana. (Deut. 10:12, 13; 30:19, 20) M’malomwake makolowo angapemphe Yehova kuti awathandize kuti azimufika pamtima mwanayo n’cholinga choti azikonda Yehova komanso kukhala naye pa ubwenzi.—Miy. 22:6; Aef. 6:4. w23.11 21 ¶5; 23 ¶12

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025

Lolemba, July 21

Pitirizani kulimbikitsana.​—1 Ates. 4:18.

N’chifukwa chiyani kutonthoza ena kumasonyeza kuti tili ndi chikondi? Buku lina lofotokoza mawu a m’Baibulo linanena kuti mawu akuti “kutonthoza” omwe Paulo anagwiritsa ntchito amatanthauza “kuima pafupi ndi munthu kuti timulimbikitse pamene wakumana ndi vuto lalikulu.” Choncho tikatonthoza m’Khristu mnzathu yemwe wakumana ndi vuto, timamuthandiza kuti aimirire n’kupitiriza kuyenda panjira yokalandira moyo. Nthawi iliyonse yomwe tatonthoza m’bale kapena mlongo, timasonyeza kuti timakonda Akhristu anzathu. (2 Akor. 7:6, 7, 13) Kutonthoza ena n’kogwirizananso ndi chifundo. N’chifukwa chiyani tikutero? Mtima wachifundo ndi umene umalimbikitsa munthu kuti atonthoze ena komanso kuwathandiza. Choncho timayamba ndi kukhala ndi chifundo, kenako timatonthoza ena. Paulo anagwirizanitsa chifundo cha Yehova ndi zimene amachita potonthoza ena. Iye ananena kuti Yehova ndi “Bambo wachifundo chachikulu ndiponso Mulungu amene amatitonthoza pa vuto lililonse.”—2 Akor. 1:3. w23.11 9-10 ¶8-10

Kuphunzira Malemba Tsiku ndi Tsiku—2025
Takulandirani.
Laibulaleyi imathandiza anthu kufufuza mabuku ofalitsidwa ndi Mboni za Yehova a m'zinenero zosiyanasiyana.
Kuti mupange dawunilodi mabuku, pitani pa jw.org.
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena