Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 10
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Deuteronomo

      • Anapanganso miyala yosema iwiri (1-11)

      • Zimene Yehova amafuna (12-22)

        • Muziopa komanso kukonda Yehova (12)

Deuteronomo 10:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 34:1

Deuteronomo 10:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 34:4

Deuteronomo 10:4

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “Mawu Khumi.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 32:15
  • +Eks 20:1; 34:28; De 4:13
  • +De 4:36; 5:4
  • +Eks 19:17; De 5:22

Deuteronomo 10:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 34:29

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    1/15/2006, tsa. 31

Deuteronomo 10:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 20:23, 24; 33:31, 38
  • +Nu 20:28

Deuteronomo 10:7

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “makhwawa a madzi.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 33:33

Deuteronomo 10:8

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 1:50; 3:6; 8:14
  • +Nu 3:30, 31
  • +Nu 6:23-27; De 21:5; 2Mb 30:27

Deuteronomo 10:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 18:20, 24; De 18:1

Deuteronomo 10:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 24:18; 34:28
  • +Eks 32:14

Deuteronomo 10:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 15:18

Deuteronomo 10:12

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mik 6:8
  • +De 5:29
  • +De 5:33; Yos 22:5
  • +De 6:5; Lu 10:27

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale, lesson 25

    Nsanja ya Olonda,

    10/1/2009, tsa. 10

Deuteronomo 10:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 6:24

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    10/1/2009, tsa. 10

Deuteronomo 10:14

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “kumwambamwamba.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Mb 29:11; Sl 24:1; 115:16

Deuteronomo 10:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 4:37

Deuteronomo 10:16

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “muchite mdulidwe wa.”

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “ndipo musaumitsenso khosi lanu.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 30:6
  • +Eks 34:9; De 9:6; 31:27

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    6/1/2007, tsa. 13

Deuteronomo 10:17

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 18:11; 2Mb 2:5; Sl 97:9
  • +Mac 10:34; Aro 2:11

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo,

    Yandikirani, tsa. 114

Deuteronomo 10:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Sl 68:5; Yak 1:27
  • +Le 19:10; De 24:14; Sl 146:9

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Yandikirani, ptsa. 113-114

Deuteronomo 10:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 22:21; Le 19:34

Deuteronomo 10:20

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Lu 4:8

Deuteronomo 10:21

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 15:2; Chv 19:6
  • +2Sa 7:23

Deuteronomo 10:22

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 46:27; Eks 1:5; Mac 7:14
  • +Ge 15:1, 5

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 10:1Eks 34:1
Deut. 10:3Eks 34:4
Deut. 10:4Eks 32:15
Deut. 10:4Eks 20:1; 34:28; De 4:13
Deut. 10:4De 4:36; 5:4
Deut. 10:4Eks 19:17; De 5:22
Deut. 10:5Eks 34:29
Deut. 10:6Nu 20:23, 24; 33:31, 38
Deut. 10:6Nu 20:28
Deut. 10:7Nu 33:33
Deut. 10:8Nu 1:50; 3:6; 8:14
Deut. 10:8Nu 3:30, 31
Deut. 10:8Nu 6:23-27; De 21:5; 2Mb 30:27
Deut. 10:9Nu 18:20, 24; De 18:1
Deut. 10:10Eks 24:18; 34:28
Deut. 10:10Eks 32:14
Deut. 10:11Ge 15:18
Deut. 10:12Mik 6:8
Deut. 10:12De 5:29
Deut. 10:12De 5:33; Yos 22:5
Deut. 10:12De 6:5; Lu 10:27
Deut. 10:13De 6:24
Deut. 10:141Mb 29:11; Sl 24:1; 115:16
Deut. 10:15De 4:37
Deut. 10:16De 30:6
Deut. 10:16Eks 34:9; De 9:6; 31:27
Deut. 10:17Eks 18:11; 2Mb 2:5; Sl 97:9
Deut. 10:17Mac 10:34; Aro 2:11
Deut. 10:18Sl 68:5; Yak 1:27
Deut. 10:18Le 19:10; De 24:14; Sl 146:9
Deut. 10:19Eks 22:21; Le 19:34
Deut. 10:20Lu 4:8
Deut. 10:21Eks 15:2; Chv 19:6
Deut. 10:212Sa 7:23
Deut. 10:22Ge 46:27; Eks 1:5; Mac 7:14
Deut. 10:22Ge 15:1, 5
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 10:1-22

Deuteronomo

10 “Pa nthawi imeneyo Yehova anandiuza kuti, ‘Useme miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija+ komanso upange likasa lamatabwa. Ukatero ukwere mʼphiri muno kwa ine. 2 Pamiyalayo ndidzalembapo mawu amene anali pamiyala yoyamba ija, imene unaiswa, ndipo udzaiike mʼlikasalo.’ 3 Choncho ndinapanga likasa la mtengo wa mthethe nʼkusema miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija. Kenako ndinakwera mʼphiri, miyala iwiriyo ili mʼmanja mwanga.+ 4 Ndiyeno analemba pamiyalayo mawu amene analemba poyamba aja,+ Malamulo Khumi,*+ amene Yehova anakuuzani paphiri kuchokera mʼmoto,+ pa tsiku limene munasonkhana kuphiri.+ Atatero, Yehova anandipatsa miyalayo. 5 Kenako ndinatembenuka nʼkutsika mʼphirimo+ ndipo ndinaika miyala iwiriyo mʼlikasa limene ndinapanga. Mpaka pano miyalayo idakali momwemo, mogwirizana ndi zimene Yehova anandilamula.

6 Zitatero Aisiraeli anachoka ku Beeroti Bene-yaakana kupita ku Mosera. Kumeneku nʼkumene Aroni anafera ndipo anamuikanso komweko.+ Mwana wake Eleazara anayamba kutumikira monga wansembe mʼmalo mwa Aroniyo.+ 7 Ndiyeno ananyamuka pamalo amenewo kupita ku Gudigoda. Anachokanso ku Gudigoda kupita ku Yotibata,+ dziko lokhala ndi mitsinje ya madzi.*

8 Pa nthawi imeneyo, Yehova anapatula fuko la Levi+ kuti lizinyamula likasa la pangano la Yehova,+ liziima pamaso pa Yehova nʼkumamutumikira komanso kuti lizidalitsa anthu mʼdzina lake+ ngati mmene akuchitira mpaka lero. 9 Nʼchifukwa chake fuko la Levi silinapatsidwe gawo kapena cholowa ngati abale awo. Cholowa chawo ndi Yehova, mogwirizana ndi zimene Yehova Mulungu wanu anawauza.+ 10 Ine ndinakhala mʼphirimo kwa masiku 40, masana ndi usiku,+ ngati mmene ndinachitira poyamba paja. Pa nthawi imeneyinso Yehova anandimvetsera.+ Yehova sankafuna kukuwonongani. 11 Kenako Yehova anandiuza kuti, ‘Tsogolera anthuwa ndipo mukonzekere ulendo, kuti akalowe nʼkutenga dziko limene ndinalumbira kwa makolo awo kuti ndidzawapatsa.’+

12 Tsopano Aisiraeli inu, kodi Yehova Mulungu wanu akufuna kuti muzichita chiyani?+ Akufuna kuti muzichita izi: muziopa Yehova Mulungu wanu,+ muziyenda mʼnjira zake zonse,+ muzikonda ndi kutumikira Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse komanso moyo wanu wonse,+ 13 ndiponso kuti muzisunga malamulo a Yehova ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero, kuti zinthu zikuyendereni bwino.+ 14 Taonani, kumwamba ndi kwa Yehova Mulungu wanu, ngakhale kumwamba kwa kumwambako* komanso dziko lapansi ndi zonse zili mmenemo zonsezo ndi zake.+ 15 Koma Yehova anayandikira kwa makolo anu okha nʼkuwasonyeza chikondi chake, ndipo wasankha inuyo mbadwa zawo+ pakati pa anthu onse, ngati mmene mulili lero. 16 Tsopano muyeretse* mitima yanu+ ndipo musakhalenso ankhutukumve.*+ 17 Chifukwa Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa milungu+ ndi Mbuye wa ambuye. Iye ndi Mulungu wamkulu, wamphamvu ndi woopsa, amene sakondera munthu aliyense+ ndipo salandira chiphuphu. 18 Iye amachitira chilungamo ana amasiye ndi akazi amasiye,+ ndipo amakonda mlendo+ moti amamupatsa chakudya ndi zovala. 19 Inunso muzikonda mlendo, chifukwa nanunso munali alendo mʼdziko la Iguputo.+

20 Yehova Mulungu wanu muzimuopa, muzimutumikira,+ muzikhala naye pafupi kwambiri komanso muzilumbira pa dzina lake. 21 Iye ndi amene muyenera kumutamanda.+ Iyeyo ndi Mulungu wanu amene wakuchitirani zinthu zazikulu ndi zochititsa mantha zonsezi, zimene mwaziona ndi maso anu.+ 22 Makolo anu anapita ku Iguputo ndi anthu 70,+ koma pano Yehova Mulungu wanu wakuchulukitsani ngati nyenyezi zakumwamba.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena