Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb17 April tsamba 2
  • Muziwalandira ndi Manja Awiri

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Muziwalandira ndi Manja Awiri
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
  • Nkhani Yofanana
  • Achititseni Kudzimva Olandiridwa pa Chikumbutso
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1994
  • Umboni Wamphamvu Udzaperekedwa
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Tidzalandire Bwino Alendo
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Alandireni Bwino
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2017
mwb17 April tsamba 2

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Muziwalandira ndi Manja Awiri

Kodi ndi ndani omwe tiyenera kuwalandira ndi manja awiriwa? Ndi aliyense amene amabwera kumisonkhano yathu. (Aroma 15:7; Aheb. 13:2) Angakhale atsopano, Mkhristu mnzathu yemwe wachokera kudziko lina kapenanso Mkhristu amene anasiya kusonkhana kwa nthawi yaitali. Taganizirani muli inuyo, kodi simungathokoze ena atakulandirani ndi manja awiri? (Mat. 7:12) Choncho, bwanji osayesa kuchita khama kuti muzipereka moni mu Nyumba ya Ufumu, misonkhano isanayambe komanso ikatha? Izi zimathandiza kuti onse mumpingo azikondana ndiponso Yehova amalemekezedwa. (Mat. 5:16) N’zoona kuti sizingatheke kulankhulana ndi aliyense. Komabe tikamayesetsa, aliyense amaona kuti walandiridwa.a

Tiyenera kulandira bwino anthu nthawi zonse osati pa nthawi ya Chikumbutso yokha. Atsopano akaona chikondi pakati pathu, amalemekeza Mulungu ndipo zimawalimbikitsa kuti ayambe kulambira nafe limodzi.​—Yoh. 13:35.

a Tiyenera kukumbukira kuti Baibulo limaletsa kulankhulana ndi anthu ochotsedwa kapena odzilekanitsa.​—1 Akor. 5:11; 2 Yoh. 10.

M’bale akulandira atsopano amene abwera ku Nyumba ya Ufumu

ZIMENE MUNGACHITE KUTI MUTHANDIZE ATSOPANO

  • Auzeni dzina lanu n’kuwapempha kuti akuuzeni lawo

  • Apempheni kuti mukhale nawo pamodzi

  • Muziona nawo limodzi Baibulo lanu komanso nyimbo

  • Pambuyo pa misonkhano muzipeza nthawi yoyankha mafunso amene angakhale nawo

  • Ngati n’kotheka mungawapemphe kuti muziphunzira nawo Baibulo

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena