PHUNZIRO 21
Kutsindika Malemba Moyenerera
PAMENE muuza ena zolinga za Mulungu, kaya panokha kapena papulatifomu, zimene mukunena zizikike m’Mawu a Mulungu. Zimenezi zimatanthauza kuŵerenga malemba m’Baibulo, kuwaŵerenga bwino.
Kutsindika Koyenerera Kumaphatikizapo Mmene Mukumvera. Malemba aziŵerengedwa ndi mzimu wake wa nkhaniyo. Talingalirani zitsanzo zotsatirazi. Pamene muŵerenga Salmo 37:11, mawu anu ayenera kusonyeza chisangalalo choyembekezera mtendere wolonjezedwa pamenepo. Poŵerenga Chivumbulutso 21:4 za kutha kwa mavuto ndi imfa, mawu anu asonyeze kuyamikira mpumulo wodabwitsa wonenedweratuwo. Mawu a pa Chivumbulutso 18:2, 4, 5, ochonderera anthu kuti atuluke mu “Babulo Wamkulu” wodzaza ndi machimo, tiwaŵerenge ndi mzimu wosonyeza kufunika kochitapo kanthu msangamsanga. Inde, kukhudzika mtima kosonyezedwako kuzichokeradi mumtima, koma kusakhale konyanyira. Kukhudzika mtima koyenerera kumadalira mawuwo ndi mmene awagwiritsira ntchito.
Tsindikani Mawu Oyenerera. Ngati mfundo yanu palemba lina ikukhudza mbali imodzi yokha ya lembalo, tsindikani mbali yokhayo poŵerenga. Mwachitsanzo, ngati mukufuna kufotokoza tanthauzo la mawu akuti “muthange mwafuna Ufumu” pa Mateyu 6:33, poŵerenga simungatsindike kwambiri mawu akuti “chilungamo chake” kapena akuti “zonse zimenezo.”
M’nkhani ya pa Msonkhano wa Utumiki, mungafune kuŵerenga Mateyu 28:19. Kodi mungatsindike mawu ati? Ngati mukufuna kulimbikitsa khama loyambitsa maphunziro a Baibulo apanyumba, tsindikani mawu akuti “phunzitsani anthu.” Koma ngati mukufuna kufotokoza udindo wa Mkristu wolalikira choonadi cha m’Baibulo kwa alendo m’dziko kapena pofuna kulimbikitsa ofalitsa ena kukatumikira kumalo osoŵa, mungatsindike mawu akuti “anthu a mitundu yonse.”
Kaŵirikaŵiri, timapereka lemba kuti liyankhe funso kapena kutsimikizira mfundo imene ena angatsutse. Ngati titsindika mofanana ganizo lililonse palemba, omvera sangathe kuona kuti likukhudzana motani ndi nkhaniyo. Mfundo yake ingakhale yoonekera bwino kwa inu koma osati kwa iwo.
Mwachitsanzo, poŵerenga Salmo 83:18 m’Baibulo lokhala ndi dzina la Mulungu, ngati mutsindika kwambiri mawu akuti “Wam’mwambamwamba,” mwininyumba angalephere kugwirapo mfundo yoonekeratu yakuti Mulungu ali ndi dzina lakelake. Tsindikani dzina lakuti “Yehova.” Komabe, pogwiritsa ntchito lemba lokhalokhalo kufotokoza ufumu wa Yehova, tsindikani kwambiri mawu akuti “Wam’mwambamwamba.” Mofananamo, poŵerenga Yakobo 2:24 kusonyeza kuti chikhulupiriro chiyenera kukhala ndi ntchito, ngati mutsindika kwambiri mawu akuti “ayesedwa wolungama” m’malo mwa “ntchito,” ena okumverani angaphonye mfundo yake.
Chitsanzo china chothandiza chili pa Aroma 15:7-13. Imeneyi ndi mbali ya kalata imene mtumwi Paulo analembera mpingo wokhala ndi Akristu osakhala Ayuda ndi Akristu achiyuda. Pamenepa mtumwi Paulo akufotokoza mfundo yakuti utumiki wa Kristu supindulitsa Ayuda odulidwa okha komanso anthu a mitundu kotero kuti “anthu a mitundu ina akalemekeze Mulungu, chifukwa cha chifundo” chake. Ndiyeno, Paulo akugwira mawu malemba anayi posonyeza mwayi wotsegukira amitunduwo. Kodi mawu ogwidwawo mungawaŵerenge motani kuti mutsindike mfundo imene Paulo anali nayo m’maganizo? Ngati mufuna kuchonga mawu oyenera kuwatsindika, mungachonge mawu akuti “anthu a mitundu ina” pavesi 9, “amitundu inu” pavesi 10, “a mitundu yonse” ndi “anthu onse” pavesi 11, ndi “anthu amitundu” pavesi 12. Ndi kutsindika koteroko, yesani kuŵerenga Aroma 15:7-13. Mmene mukutero, mudzatha kumveketsa bwino lomwe kalingaliridwe ka Paulo pamfundo zake.
Njira Zotsindikira. Mawu opereka ganizo limene mukufuna kuunika akhoza kutsindikidwa m’njira zingapo. Njira imene muigwiritse ntchito ikhale yogwirizana ndi lembalo komanso nkhani yake. Nazi njira zingapo.
Kutsindika ndi liwu. Izi zimachitika mwa kusintha kamvekedwe ka liwu kumene kumachititsa mawu opereka ganizo lofunikira kuonekera kwambiri m’sentensi. Kutsindikako kumachitika mwa kusintha liwu—kulikweza kapena kulitsitsa. M’zinenero zambiri, amatsindika mawu mwa kukweza kapena kutsitsa liwu. Koma m’zinenero zina, kuchita zimenezo kungasinthiretu tanthauzo la mawu. Nthaŵi zina timalankhula pang’onopang’ono pofuna kumveketsa bwino mawu ofunikira. Kuteroko kumawonjezera ulemerero wa mawuwo. M’zinenero zosatsindika ganizo mwa kukweza kapena kutsitsa liwu pofuna kugogomeza mawu ofunika, m’pofunika kugwiritsa ntchito njira zina za chinenerocho kuti mumveketse mfundo zofunikira.
Kupuma. Mungapume musanaŵerenge kapena mutaŵerenga mbali yofunikira ya lemba—kapena ponse paŵiri. Kupuma musanaŵerenge ganizo lalikulu kumadzutsa chidwi; kupuma pambuyo pake kumakhomereza ganizolo. Koma ngati mupuma pafupipafupi kwambiri, palibe chimaoneka chapadera.
Kubwereza mawu. Mutha kutsindikanso mwa kudzidula ndi kuŵerenganso mawuwo. Koma njira imene ambiri amagwiritsa ntchito ndiyo ya kumaliza lemba lonse kenako n’kutchulanso mawu ofunikirawo.
Manja ndi nkhope. Kachitidwe ka manja ndi nkhope ndi thupi lonse kaŵirikaŵiri kamawonjezera mzimu wa mawu.
Kamvekedwe ka liwu. M’zinenero zina, mawu angaŵerengedwe ndi liwu logwirizana ndi tanthauzo lake. Apanso m’pofunika kusamala, makamaka kupeŵa kulankhula mozaza.
Pamene Ena Aŵerenga Malemba. Pamene mwininyumba aŵerenga lemba, angatsindike mawu olakwika kapena sangatsindike alionse. Kodi mungatani pamenepo? Mungamveketse tanthauzo la lembalo mwa kufotokoza cholinga chake. Mutatero, mungaunike mwachindunji mawu opereka ganizo lofunikawo m’Baibulo.