Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 March tsamba 5
  • Yobu Anasonyeza Kukhumudwa Kwake

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yobu Anasonyeza Kukhumudwa Kwake
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Yobu Anapirira—Nafenso Tingatero!
    Nsanja ya Olonda—1994
  • Yobu Analemekeza Dzina la Yehova
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Mfundo Zazikulu za M’buku la Yobu
    Nsanja ya Olonda—2006
  • “Yembekezera Yehova”
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2022
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 March tsamba 5

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | YOBU 6-10

Yobu Anasonyeza Kukhumudwa Kwake

AnzakeYobu atatu

Yobu anakhalabe wokhulupirika ngakhale kuti chuma chake chonse chinatha, ana ake onse anafa komanso anadwala kwambiri. Koma Satana anayesetsabe kuchita zinthu zoipa n’cholinga choti Yobu akhumudwe n’kusiya kutumikira Yehova. Tsiku lina kunyumba kwa Yobu kunabwera “anzake” atatu. Anzakewo atafika, anachita zinthu zosonyeza kuti akumumvera chisoni. Iwo anakhala naye limodzi masiku 7, popanda kumuyankhula chilichonse. Pambuyo pake anayamba kuyankhula zinthu zosonyeza kuti Yobu anali wolakwa.

Yobu anakhalabe wokhulupirika kwa Yehova ngakhale kuti panali zofooketsa zambiri

6:3; 7:16; 9:20-22; 10:1, 12

  • Chifukwa chowawidwa mtima kwambiri ndi mavuto, Yobu anayamba kuona zinthu molakwika. Anaganiza kuti Mulungu analibe nazo ntchito ngakhale kuti iye anayesetsa kukhala wokhulupirika

  • Chifukwa chokhumudwa, Yobu sanaganizire kuti pangakhale zifukwa zina zimene zikanachititsa kuti avutike

  • Ngakhale kuti anali ndi chisoni kwambiri, Yobu anauza anzake amene ankamuimba mlanduwo kuti iye ankakondabe kwambiri Yehova

Yobu ali ndi zilonda thupi lonse
    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena