10 koma makamaka anthu amene amafunafuna kugonana ndi anthu ena n’cholinga choti awaipitse,+ ndiponso amene amanyoza owalamulira.+
Anthu amenewa ndi opanda mantha ndiponso ndi omva zawo zokha, ndipo sanjenjemera ndi anthu aulemerero. M’malomwake, amalankhula zinthu zowanyoza.+