2 Ndikukulemberani inu amene Mulungu Atate+ anakudziwiranitu mwa kukuyeretsani ndi mzimu+ kuti mukhale omvera ndi owazidwa+ magazi a Yesu Khristu, kuti:+
Kukoma mtima kwakukulu ndi mtendere ziwonjezeke kwa inu.+
7 Komatu, ngati tikuyenda m’kuunika ngati mmene iye alili m’kuunika,+ ndiye kuti ndife ogwirizana,+ ndipo magazi+ a Yesu Mwana wake akutiyeretsa+ ku uchimo wonse.+
5 Komanso, kuchokera kwa Yesu Khristu, “Mboni Yokhulupirika,”+ “Woyamba kubadwa kuchokera kwa akufa,”+ ndiponso “Wolamulira wa mafumu a dziko lapansi.”+
Kwa iye amene amatikonda,+ amenenso anatimasula ku machimo athu ndi magazi ake enieniwo,+