2 Sihoni+ mfumu ya Aamori, yemwe ankakhala ku Hesiboni.+ Dera lomwe anali kulamulira linkayambira pakatikati pa chigwa cha Arinoni kuphatikizapo mzinda wa Aroweli,+ umene unali m’mphepete mwa mtsinje wa Arinoni,+ mpaka hafu ya Giliyadi kukalekezera kuchigwa cha Yaboki,+ kumalire ndi ana a Amoni.