28“Koma iwe patula Aroni m’bale wako pamodzi ndi ana ake pakati pa ana a Isiraeli, ndipo Aroniyo+ atumikire monga wansembe wanga pamodzi ndi ana akewo,+ Nadabu, Abihu,+ Eleazara ndi Itamara.+
2 “Tenga Aroni pamodzi ndi ana ake,+ zovala zawo,+ mafuta odzozera,+ ng’ombe yamphongo ya nsembe yamachimo,+ nkhosa ziwiri zamphongo, ndi dengu la mikate yopanda chofufumitsa.+