16 Awa ndi mayina a ana aamuna a Levi,+ malinga ndi mzere wobadwira wa makolo awo:+ Gerisoni, Kohati ndi Merari.+ Ndipo Levi anakhala ndi moyo zaka 137.
4 Atachita maere, maerewo anagwera mabanja a Akohati.+ Choncho mizinda 13 inakhala ya ana a wansembe Aroni, omwe anali Alevi. Mizinda yake inachokera m’mafuko a Yuda,+ Simiyoni,+ ndi Benjamini.+