6 Tsopano tabwerani chonde, mudzanditembererere+ anthuwa chifukwa ndi amphamvu kuposa ineyo, kuti mwina ndingawagonjetse n’kuwapitikitsa m’dziko lino. Ndikudziwa kuti munthu amene inu mwamudalitsa, amakhaladi wodalitsika, ndipo munthu amene mwamutemberera, amakhaladi wotembereredwa.”+