9 Chotero Esau anapita kwa Isimaeli* n’kukatengako mkazi kuwonjezera pa akazi amene anali nawo.+ Mkaziyo dzina lake anali Mahalati, ndipo anali mlongo wake wa Nebayoti. Mahalati anali mwana wa Isimaeli, mwana wa Abulahamu.
7 Nkhosa zonse za ku Kedara+ zidzasonkhanitsidwa kwa iwe. Nkhosa zamphongo za ku Nebayoti+ zidzakutumikira.+ Ine ndidzazilandira paguwa langa lansembe,+ ndipo ndidzakongoletsa nyumba yanga yokongola.+