11 Tsopano anzake atatu a Yobu anamva za tsoka lonse limene linamugwera ndipo aliyense wa iwo anabwera kuchokera kwawo. Mayina awo anali Elifazi wa ku Temani,+ Bilidadi wa ku Shuwa+ ndi Zofari wa ku Naama.+ Iwo anakumana pamodzi atachita kupangana+ kuti apite kukazonda Yobu ndi kukamulimbikitsa.+