-
2 Mafumu 18:4Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
4 Hezekiya ndiye anachotsa malo okwezeka,+ kugwetsa zipilala zopatulika,+ ndi kudula mzati wopatulika.+ Iye anaphwanyaphwanya njoka yamkuwa+ imene Mose anapanga,+ chifukwa pofika masiku amenewo, ana a Isiraeli anakhala akufukiza nsembe+ yautsi kwa njoka yamkuwayo, ndipo inkatchedwa fano la njoka yamkuwa.+
-
-
Ezekieli 8:3Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
3 Kenako iye anatambasula chinachake chooneka ngati dzanja+ ndipo anagwira tsitsi la kumutu kwanga n’kundinyamula. Ndiyeno mzimu+ unandinyamulira m’malere, pakati pa dziko lapansi ndi kumwamba, n’kundipititsa ku Yerusalemu m’masomphenya a Mulungu.+ Unandifikitsa pakhomo la kanyumba ka pachipata cha bwalo lamkati+ choyang’ana kumpoto. Pamenepo m’pamene panali kukhala chizindikiro choimira nsanje, chimene chinali kuchititsa Mulungu nsanje.+
-