-
Numeri 29:6Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
6 Muzipereka nsembe zimenezi kuwonjezera pa nsembe yopsereza+ ya mwezi ndi mwezi, limodzi ndi nsembe yake yambewu.+ Muzizipereka kuwonjezeranso pa nsembe yopsereza+ ya tsiku ndi tsiku, limodzi ndi nsembe yake yambewu,+ limodzinso ndi nsembe zachakumwa.+ Muzipereka nsembe zopserezazo malinga ndi dongosolo lake la nthawi zonse, monga nsembe zotentha ndi moto zopereka fungo lokhazika mtima pansi kwa Yehova.+
-
-
2 Mbiri 8:13Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
13 Anapereka nsembezo mogwirizana ndi dongosolo la tsiku ndi tsiku+ loperekera nsembe, malinga ndi chilamulo cha Mose. Nsembezo zinali za pa masabata,+ za pa masiku okhala mwezi,+ ndi za pa zikondwerero zoikidwiratu+ zochitika katatu pa chaka.+ Zikondwererozo zinali chikondwerero cha mikate yopanda chofufumitsa,+ chikondwerero cha masabata,+ ndi chikondwerero cha misasa.+
-