Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Numeri 28:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 “‘Kumayambiriro kwa mwezi uliwonse, muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Nsembeyo izikhala ng’ombe ziwiri zazing’ono zamphongo, nkhosa imodzi yamphongo, ndi ana a nkhosa 7 amphongo opanda chilema. Mwana wa nkhosa aliyense azikhala wachaka chimodzi.+

  • Numeri 29:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 6 Muzipereka nsembe zimenezi kuwonjezera pa nsembe yopsereza+ ya mwezi ndi mwezi, limodzi ndi nsembe yake yambewu.+ Muzizipereka kuwonjezeranso pa nsembe yopsereza+ ya tsiku ndi tsiku, limodzi ndi nsembe yake yambewu,+ limodzinso ndi nsembe zachakumwa.+ Muzipereka nsembe zopserezazo malinga ndi dongosolo lake la nthawi zonse, monga nsembe zotentha ndi moto zopereka fungo lokhazika mtima pansi kwa Yehova.+

  • 1 Mbiri 23:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Anali kutumikiranso nthawi iliyonse yopereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa masabata,+ pa masiku okhala mwezi,+ ndi pa nyengo za chikondwerero.+ Nthawi zonse anali kutumikira popereka nsembezo kwa Yehova, malinga ndi ziwerengero zake, komanso potsata lamulo lake.

  • 2 Mbiri 8:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Anapereka nsembezo mogwirizana ndi dongosolo la tsiku ndi tsiku+ loperekera nsembe, malinga ndi chilamulo cha Mose. Nsembezo zinali za pa masabata,+ za pa masiku okhala mwezi,+ ndi za pa zikondwerero zoikidwiratu+ zochitika katatu pa chaka.+ Zikondwererozo zinali chikondwerero cha mikate yopanda chofufumitsa,+ chikondwerero cha masabata,+ ndi chikondwerero cha misasa.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena