Salimo 93:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Mpando wanu wachifumu unakhazikika kalekale.+Munakhalako kuyambira kalekale.+ Yesaya 40:28 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 28 Kodi iwe sukudziwa kapena kodi sunamve?+ Yehova, Mlengi wa malekezero a dziko lapansi, ndiye Mulungu mpaka kalekale.+ Iye satopa kapena kufooka.+ Palibe amene angadziwe zimene iyeyo amazimvetsa.+ Yesaya 45:22 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 22 “Tembenukirani kwa ine kuti mupulumuke,+ inu nonse amene muli kumapeto kwa dziko lapansi, pakuti ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.+ Yeremiya 10:10 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 10 Koma Yehova ndi Mulungu woonadi.+ Iye ndi Mulungu wamoyo+ ndipo ndi Mfumu mpaka kalekale.+ Dziko lapansi lidzagwedezeka ndi mkwiyo wake,+ ndipo palibe mitundu ya anthu imene idzalimbe pamene iye akuidzudzula.+ Habakuku 1:12 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 12 Inu Yehova, inutu mwakhalapo kuyambira kalekale.+ Inu Mulungu wanga, Mulungu wanga Woyera, inu simufa.+ Inu Yehova, mwaika Akasidi pamalo oti muwaweruze. Inu Thanthwe,+ mwasankha kuti mutidzudzule.+ 1 Timoteyo 1:17 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 17 Kwa Mfumu yamuyaya,+ imene siifa,+ yosaoneka,+ yekhayo amene ali Mulungu,+ kwa iyeyo kupite ulemu ndi ulemerero mpaka muyaya.+ Ame. Chivumbulutso 1:8 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 “Ine ndine Alefa ndi Omega,”*+ akutero Yehova Mulungu, “Iye amene alipo, amene analipo, ndi amene akubwera,+ Wamphamvuyonse.”+ Chivumbulutso 15:3 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 3 Iwo akuimba nyimbo ya Mose+ kapolo wa Mulungu, ndi nyimbo ya Mwanawankhosa,+ yakuti: “Ntchito zanu n’zazikulu ndi zodabwitsa,+ inu Yehova Mulungu Wamphamvuyonse.+ Njira zanu ndi zolungama ndi zoona,+ inu Mfumu yamuyaya.+
28 Kodi iwe sukudziwa kapena kodi sunamve?+ Yehova, Mlengi wa malekezero a dziko lapansi, ndiye Mulungu mpaka kalekale.+ Iye satopa kapena kufooka.+ Palibe amene angadziwe zimene iyeyo amazimvetsa.+
22 “Tembenukirani kwa ine kuti mupulumuke,+ inu nonse amene muli kumapeto kwa dziko lapansi, pakuti ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.+
10 Koma Yehova ndi Mulungu woonadi.+ Iye ndi Mulungu wamoyo+ ndipo ndi Mfumu mpaka kalekale.+ Dziko lapansi lidzagwedezeka ndi mkwiyo wake,+ ndipo palibe mitundu ya anthu imene idzalimbe pamene iye akuidzudzula.+
12 Inu Yehova, inutu mwakhalapo kuyambira kalekale.+ Inu Mulungu wanga, Mulungu wanga Woyera, inu simufa.+ Inu Yehova, mwaika Akasidi pamalo oti muwaweruze. Inu Thanthwe,+ mwasankha kuti mutidzudzule.+
17 Kwa Mfumu yamuyaya,+ imene siifa,+ yosaoneka,+ yekhayo amene ali Mulungu,+ kwa iyeyo kupite ulemu ndi ulemerero mpaka muyaya.+ Ame.
8 “Ine ndine Alefa ndi Omega,”*+ akutero Yehova Mulungu, “Iye amene alipo, amene analipo, ndi amene akubwera,+ Wamphamvuyonse.”+
3 Iwo akuimba nyimbo ya Mose+ kapolo wa Mulungu, ndi nyimbo ya Mwanawankhosa,+ yakuti: “Ntchito zanu n’zazikulu ndi zodabwitsa,+ inu Yehova Mulungu Wamphamvuyonse.+ Njira zanu ndi zolungama ndi zoona,+ inu Mfumu yamuyaya.+