11 Inu Yehova, ukulu,+ mphamvu,+ kukongola,+ ulemerero,+ ndi ulemu+ ndi zanu, chifukwa zinthu zonse zakumwamba ndi za padziko lapansi ndi zanu.+ Ufumu+ ndi wanu, inu Yehova, ndinunso Wokwezeka monga mutu pa onse.+
5 Ine ndinati: “Tsoka kwa ine! Popeza maso anga aona Mfumu, Yehova wa makamu.+ Nditsikira kuli chete pakuti ndine munthu wa milomo yodetsedwa,+ ndipo ndikukhala pakati pa anthu a milomo yodetsedwa.”+