2 Kweza maso ako ndi kuona njira zodutsidwadutsidwa.+ Ndi pamalo ati pamene amuna sanakugonerepo?+ Unali kukhala m’mbali mwa njira kudikirira okondedwa ako, ngati mmene Mluya amakhalira m’chipululu.+ Ukuipitsa dzikoli ndi zochita zako zauhule komanso kuipa kwako.+